Vichito 1
1
1Wolemekezeka Teofelio,
mchikalakala changa icho nidachogolela kulemba nidakulembela nghani zonjhe izo wadazichita Yesu ni wadaziyaluza kuyambila mmayambo mwa njhito zake, 2mbaka siku lijha wadanyakulidwa kupita kumwamba. Wakali wosanyakulidwe kupita kumwamba, Yesu wadaapacha maagizo atumwi wajha wadaasangha kupitila Mzimu Woyela. 3Ndhawi ya siku alobaini Pambuyo pa nyifa yake, Yesu wadajhilangiza kwawo ni kwaachimikizila mnjila zambili kuti iye wali wa moyo, anyiiwo adamuona ni wadakamba nawo nghani za Ufumu wa Mnungu. 4Nyengo ina yapo wamadya chakudya pamojhi nawo, wadaapacha lamulo ili, “Msadachoka mu Yelusalemu muno, nambho mlindilile ahadi ya Mzimu woyela uwo mwanivela ninikamba nghani zake. 5Yohana wadaabatiza wandhu kwa majhi, nambho posachedwa simubatizidwe kwa Mzimu Woyela.”
Yesu wanyakulidwa kupita kumwamba
Maluko 16:19-20; Luka 24:50-53
6Ndiipo atumwi adasonghana kumzungulila Yesu ni adamfunjha, “Ambuye, bwanji iyi nde ndhawi ya kwaabwezela a Izilaeli ufumu wao?”
7Yesu wadayangha, “Atate wokha ndeyawo ajhiwa ndhawi ni nyengo, osati njhito yanu kujhiwa kuti siyachokele liti. 8Nambho simujhazidwe mbhavu yapo siwajhe kwanu Mzimu woyela, ni anyiimwe simukhale amboni wanga mmijhi ya Yelusalemu, Yudea yonjhe ni Samaliya, ni jhiko lonjhe lapanjhi.” 9Yapo wadamaliza kukamba chimwecho, Yesu wadanyakulidwa kupita kumwamba uku wonjhe naapenya, ni mtambo udamvinikila kuti saadamuonanjho.
10Maso yawo yapo yadali yakali kumpenyechecha kumwamba Yesu yapo wamapita, mwachizulumukila wachimuna awili yawo adavala njhalu zoyela adaima pambhepete pawo, 11adakamba, “Anyiimwe wandhu a ku Galilaya, ndande yanji muima pamenepo uku nimpenya kumwamba? Yesu uyo watengedwa kupita kumwamba, siwajhenjho ngati mujha mwamuwonela niwapita kumwamba.”
Matiya watenga malo ya Yuda
Matayo 27:3-10
12Ndiipo atumwi wajha adabwelela ku Yelusalemu kuchokela ku phili ilo litanidwa pili la Mizeituni, utali wake pafupi kilomita imojhi kuchokela ku mujhi wa Yelusalemu. 13Anyiiwo yapo adalowa mu mumbwani, adapita ku golofa mbaka ku chumba icho amakhala. Wandhu yawo adalipo adali Petulo ni Yohana ni Yakobo ni Anduleya ni filipo ni Tomaso ni Batolomayo ni Matayo ni Yakobo mwana wa Alufayo ni Simoni uyu watanidwanjho Zelote, mate yake uyo wabulanila jhiko lake, ni Yuda mwana wa Yakobo. 14Anyiyawa wonjhe adaendekela kupezana pamojhi kupembhela. Pakati pawo padali ni Maliya maye wake wa Yesu ni waachikazi wina, ni pamojhi ni achabale wake a Yesu.
15Pandhawi zimenezo, okhulupilila mia mojha ni ishilini adasonghana pajha, Petulo wadaima pakati pao ni kukamba, 16“Okhulupila achanjanga, imafunika malembo yakwanile yayo yadalosedwa ni Mzimu Woyela kupitila Daudi, wadalosa nghani za Yuda uyo wadaachogoza wandhu wajha adamgwila Yesu. 17Yuda wadali mmojhi wathu, pakuti iye naye wadasanghidwa ni Yesu kuti wachite njhito pamojhi ni ife.”
18Yuda wadagula munda kwa kutumila zijha ndalama wadazipata kuchokana ni vichito vake voipa, wadagwa mmunda mmenemo, wadang'ambika ni matumbo yake yadamwazikila kubwalo. 19Kila mundhu ku Yelusalemu wadavela nghani za nyifa ya Yuda. Chimwecho, adapatana pamalo pajha kwa mkambo wao, Akelidama, mate yake, “Munda wa Mwazi.”
20Petulo wadakamba, “Pakuti yaya yadalembedwa mchikalakala cha Zabuli,
‘Nyumba yake ikhale ya umbhawi,
pasadakhalapo mundhu wokhala mnyumba mmenemo.’ Chimchijha yalembedwa,
‘Njhito yake ya utumiki itengedwe ni mundhu mwina.’”
21“Chimwecho, ifunika timsanghe mundhu mwina pakati pa wandhu wajha ali pamojhi ni ife ndhawi zonjhe yapo Ambuye Yesu wamayenda pamojhi ni ife, 22kuyambila Yohana yapo wadambatiza Yesu mbaka siku ilo Yesu wadanyakulidwa kupita ku Mwamba. Niiye wafunika wakhale mboni wa kuhyuka kwa Yesu pamojhi ni ife.”
23Chimwecho anyiiwo adaasangha wachimuna awili, Yusufu, uyo watanidwa Balisaba uyo chimchijha wamatanidwa Yusito pamojhi ni Matiya. 24Ndiipo anyiiwo adampembha Mnungu, “Ambuye, imwe muyajhiwa maganizo ya kila mmojhi, chipano tilangizeni uyo mwamsangha pakati pa wandhu anyiyawa awili, 25kuti wachite njhito iyo wadaisiya Yuda ni kupita ku malo yayo wadafunika kupita.” 26Ndiipo wadaachitila gudugudu, Matiya wadasanghidwa ni kuongezedwa kwa anyiwajha atumwi khumi ni mmojhi.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 1: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.