Vichito Uchogoleli wa chikalakala cha vichito
Uchogoleli wa chikalakala cha vichito
Chikalakala cha vichito vifotokozela umo gulu la wandhu yao amkhulupilila Yesu Kilisito lidayambila ku Yelusalemu, ni kuenela mu Uyahudi ni ku Samaliya ni mmaiko ina, ngati umo Yesu wadaakambila Oyaluzidwa wake yapo wadali wakali siwadanyakulidwe kupita kumwamba, vichito 1:8. Chikalakala ichi chidalembedwa ni Luka uyo wadalembanjho chikalakala cha Luka. Uyu wadali sing'anga, naye wadali osunga nghani wa bwino kwa kulemba vindhu ivo vidali va uzene. Uyo wadalemba vikalakala ivi vonjhe viwili, injili ni chikalakala cha vichito, wadali Mgiliki uyo wadatanidwa, Teofolio. Nambho ikhozeka kuti vikalakala ivi vonjhe vidalembedwa ndande ya Akilisito, yawo adali Ayahudi ni Agiliki.
Chikalakala cha Vichito chidalembedwa mchaka cha 60 mbaka 64 pambuyo pa kubadwa kwa Yesu Kilisito, pakuti chikalakala chithela yapo Poolo wakali siwadamasulidwe kuchoka mndende. Luka wadamanga ulendo pamojhi ni mtumwi Poolo, chimwecho ikhozekana wadalemba chikalakala cha Vichito ku mujhi wa Atiyokiya. Chikalakala cha Vichito ni muendekelo wa chikalakala cha Luka, chiyamba kufotokozela kunyakulidwa kwa Yesu kupita kumwamba. Dala la Luka kulemba chikalakala ichi lioneka kuti ni lilijha ilo wadalinalo yapo wamalemba Injili ya Luka. Wadafuna Teofolio, ni Akilisito ambili yawo amachuluka apate uzene wa yajha amayaluzidwa. Chimwecho wadalemba kwa uzene nghani za ukhalo wa Yesu ni kuenela kwa Ukilisito.
Chikalakala cha Vichito chitipacha chifani cha umo lidali gulu la wandhu yao amkhulupilila Yesu woyamba, ni umo wandhu adakhalila kwa kumkhulupilila Yesu. Vifani va atumwi vitilangiza ifunika kukhulupilila mbhavu za Mzimu Woyela pakuyeneza Uthenga wa Injili kwa wandhu wina.
Yayo yali muchikalakala ichi
Poyamba mzimu woyela wajhela Oyaluzidwa ni gulu la wandhu yao amkhulupilila Yesu kuyamba kukula ni kuchuluka 1:1; 8:1
Ndiipo gulu la wandhu yao amkhulupilila Yesu lipita munyengo za mavuto, ni Ukilisito uenela kupitilila malile ya Yelusalemu. 8:2; 12:23
Pambuyo pake Poolo wapita ku ulendo wake woyamba ya kulalikila Uthenga Wabwino 12:24; 14:28
Ndiipo bwalo likomana ku Yelusalemu kulamula kuti vindhu viti vabwino ivo vifunika kwa wandhu yawo angokhulupililape. 15:1-35
Icho chichatila, Poolo wapita ku ulendo wake wa utumiki. 15:36; 18:22
Pambuyo pa yameneyo Poolo wadapita ku ulendo wake wakatatu wa kuuzila Uthenga Wabwino. 18:23; 20:38
Pambuyo pake Poolo wadagwilidwa yapo wadali ku Yelusalemu. 21-26
Pothela, Poolo wapelekedwa ku Loma 27:28
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito Uchogoleli wa chikalakala cha vichito: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.