Vichito 17
17
Wandhu abulana ku Sesalonike
1Poolo ni Sila adamanga ulendo kwa kupitila mijhi ya Amfipoli ni Apoloniya. Adafika kumujhi wa Tesalonike uko kudali nyumba yokomanilana Ayahudi. 2Poolo wadalowa mnyumba yokomanilana Ayahudi, ngati umo lidali khalidwe lake. Wadakambilana ni wandhu nghani za Malembo Yoyela kwa Masiku yatatu yo Pumulila wadaakambila, 3uku ni wafotokozela malembo kwa kualangiza kuti Kilisito wamafunika kufa ni kuhyuka, niwakamba, “Uyu Kilisito nikukambilani nghani zake nde Yesu.” 4Ayahudi akumojhi adaakhulupilia Poolo ni Sila ni adalamula kulunjana nawo. Chiwelengelo chidachuluka cha Agiliki yawo amamlambila Mnungu wazene ni wachikazi ambili yawo amalemekezedwa mjhiko limenelo naonjho adalunjana nawo.
5Nambho Ayahudi wina adali ni njhanje, adaatenga wandhu woipa apamalo yapo wandhu amasonhgana, adalunjhana nawo ni kuyamba kupeleka chiwawa. Adapanga gulu ni kuyambicha chiwawa mmujhi. Adapita kukhomo kwa Yasoni kwaafunafuna Poolo ni Sila, kuti waapeleke pachogolo pa wandhu. 6Nambho saadakomane, adamgwila Yasoni pamojhi ni wandhu wina yawo adamkhulupila Kilisito ni kumkwekweta mbaka kwa azee a mujhi ujha uku niapokosela, niakamba, “Wandhu anyiyawa ayambicha chiwawa kila kumalo pajhiko lonjhe, ni chipano afikanjho pamujhi pathu pano, 7ni Yasoni watokwaasunga mnyumba mwake. Anyiiwo onjhe achuchana ni lamulo la mfumu wa ku Loma, uku niakamba kuti kuli mfumu mwina, uyo watanidwa Yesu.” 8Achogoleli amujhi ni gulu la wandhu Yapo adavela chimwechi, adakwiya kupunda. 9Wadaakakamiza Yasoni ni wandhu wina yawo adamkhulupilila Yesu achoche ndalama, ndiipo adaasiya apite.
Poolo ni Sila apita ku Beloya
10Usiku yapo udafika, wajha adamkhulupilila Yesu adaakambila Poolo ni Sila ajhipita ku mujhi wa Beloya. Yapo adaifika kumeneko, adalowa mu nyumba yokomanilana Ayahudi. 11Ayahudi anyiyawa a ku Beloya amavechecha kupunda kupitilila wajha aku Sesalonike. Adakondwa kupunda yapo adauvela uthenga uwo adakambidwa ni Poolo, ni kila siku amatosoma Malembo ya Mnungu, kuona nagati icho wamakamba Poolo ni chazene. 12Nambho Ayahudi ambili pamojhi ni wachikazi ni waachimuna a Chigiliki yawo adali achogoleli, adamkhulupilila Yesu. 13Nambho Ayahudi aku Sesalonike yapo adajhiwa kuti Poolo wamatolalikila Uthenga wa Mnungu mu mujhi wa Beloya, chimchijha adalamula kupita kumeneko. Yapo adafika adachita chiwawa ni kusongezela magulu ya wandhu. 14Pampajha wajha adamkhulupilila Yesu adampelekeza Poolo mbhepete mwanyanja, nambho Sila ni Timoseo adakhalila ku Beloya. 15Wajha adampelekeza Poolo, adampelekeza mbaka kumujhi wa Asene. Ndiipo adamsiya, adabwela ku mujhi wa Beloya ni uthenga kuchokela kwa Poolo, Sila ni Timoseo kuti amchate chisanga.
Poolo walalikila mawu la Mnungu ku mujhi wa Asene
16Poolo yapo wamaalindilila Sila ni Timoseo mumujhi wa Asene, wadakwiya kupunda ndande wadaona mujhi ujha wachuluka viboliboli va minungu. 17Chimwecho wadafujhana ni Ayahudi ni wina yawo adali osati Ayahudi mu manyumba yao yokomanilana. Chimchijha siku zonjhe wamakamba ni wandhu yawo amakoma pa danga yayo amakomanilana wandhu ambili. 18Ndiipo wina yawo amachata ukhalo wa Epukolio ni Asitoiko yawo adali asomi waakulu kupunda adachuchana ni Poolo. Wina adakamba, “Bwanji mundhu uyu wakamba icho siwachijhiwa?”
Wina adakamba, “Iyeyu waoneka ngati wakamba nghani za minungu yachilendo.” Adakamba chimwechi ndande Poolo wamalalikila nghani za Yesu ni kuhyuka kwake. 19Ndiipo adamtenga Poolo ni kupitananayo khumbi ilo limatanidwa Aleopago, niakamba, “Chonde tifokotezelele ganizo ili la chipano ilo uliyaluza. 20Ivo uvikamba kwatu ni vachilendo, tifuna tijhiwe mate ya vindhu vimenevo.” 21Wandhu aku Asene ni alendo yawo amakhala mmenemo, amatumia ndhawi yao yonjhe kukambilana ni kuvechela maganizo yajha yachipano.
22Poolo wadaima pachogolo pa khumbi limenelo la Aleopago niwakamba, “Anyiimwe wandhu aku Asene! Icho nichiona pano ilangiza kuti anyiimwe ni wandhu muilambila kupunda minungu yanu. 23Yapo nimapita mmujhi wanu uku ni uko nidapenya viboliboli va minungu yanu, nikulambila kwanu, nidaona ghuwa limojhi ilo lalembedwa, ‘Kwa mnungu uyo siwajhiwika.’ Ilangiza kuti Mnungu Uyo mumlambila simumjhiwa. Chipano nifuna nikukambileni nghani za Mnungu wa uzene uyo ifunika mumlambile. 24Nde Mnungu uyo wadaumba jhiko ni vindhu vonjhe vili mkati mwake, ni Ambuye a kumwamba ni jhiko lapanjhi ni siwakhala mnyumba yamangidwa ni wandhu. 25Iye ndeuyo waapacha wandhu umoyo, mpuyo ni kila chindhu icho achifuna. Siwafuna chithandizo chilichonjhe kuchokela kwa wandhu, iye wali ni kila kandhu icho wandhu achifuna. 26Mnungu wadayamba kumuumba mundhu mmojhi, ni kupitila kwaiye wadaumba mafuko yonjhe yosiyanasiyana, ni kwaachita akhale malo yonjhe pajhiko. Wadalamula kuchokela poyamba, ndhawi iti ni kuti sakhale wandhu ameneo. 27Mnungu wadachita chimwechi kuti wandhu amfunefune iye ata ngati kwa kupambasa ni ayese kumpata, pakuti siwakhala kutali ni kila mmojhi wathu, 28ngati umo wadakambila mundhu mwina,
‘Mkati mwake ife tikhala, tijhikoza ni tilipo.’
Ngati wandhu wina umo adakambila,
‘Ife nafenjho ni wana wake.’
29Uzene ni kuti ife taonjhe ni wana a Mnungu ni tachokela kwa Mnungu. Chimwecho, tisadaganiza kuti Mnungu walingana ni viboliboli va myala ya mtengo wa ukulu, kapina ndalama kapina vamwala uwo wakonjedwa kwa kusoma ni njelu za mundhu. 30Mnungu wadachita ngati siwapenya ndhawi zijha wandhu samamjhiwe Mnungu wa zene. Nambho chipano walamula wandhu wonjhe akila kumalo alape ni kumng'anamukila iye, 31pakuti waika siku ilo siwalilamule jhiko lonjhe kwa haki kupitila mundhu uyo wadamsanghula. Iye walangiza wandhu padanga chindhu chimenecho kwa wandhu pakumuhyukicha Kilisito!”
32Yapo adavela Poolo niwakamba nghani za kuhyuka, wina wao adayamba kumseka. Nambho wina wao adakamba, “Tifuna kuivelanjho ghani imeneyo.” 33Chimwecho Poolo wadaasiya ni kuchoka. 34Nambho wandhu wina adachatana ni Poolo ni kumkhulupilila Kilisito. Pakati pawo padali Dionisio mundhu wa khumbi la Leopago ni wamkazi mmojhi uyo wadatanidwa Damali ni wandhu wina.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 17: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.