Yohana 7

7
Yesu siwakhulupilidwa ni achabale wake
1Pambuyo pa yameneyo, Yesu wadachita njhito mmalo ya mbili ya Galilaya. Siwamafune kupita ku Yudea ndande achogholeli wa Ayahudi amafuna kumpha. 2Ndhawi imeneyo Phwando la Ayahudi la Visakasa yani kukumbukila kusamuka samuka kuphululu lidawandikila, 3ndiipo, achabale wake adamkambila, “Uchokepo pano upite ku Yudea dala oyaluzidwa wako azione njhito izo uchita. 4Mundhu siwachita vindhu ko bisika ngati wafuna kujhiwika ni wandhu. Pakuti uchita vindhu ivi, chipano jhijhiwiche pajhiko la panjhi.” 5Ndande ata achabale wake sadamkhulupilile.
6Ndiipo Yesu wadaakambila, “Ndhawi yanga iyo ifunika ikali yosafike. Nambho anyiimwe ndhawi yanu ilipo sikuzonjhe. 7Wandhu apajhiko saakhoza kukuipilani anyiimwe, nambho ine aniipila ndande nachocha umboni wa vindhu ivo avichita ni voipa. 8Anyiimwe mapitani kuphwando. Ine sinipita kuphwando limenelo, ndande ndhawi yanga siida fike.” 9Yapo wadakamba yameneyo, wadakhalila ku Galilaya.
Yesu kuphwando la visakasa
10Achabale wake yapo adapita kuphwando, Yesu nayo wadapita kuphwando, nambho wadapita kwa chisisi. 11Chimwecho achogholeli wa Ayahudi amato mfunafuna pa phwando limenelo, adafunjhila, “Wali kuti mundhu yujha?”
12Kudali ni kung'olong'ota kwambili kuusu Yesu pakati pa gulu la wandhu. Akumojhi wao adakamba, “Mundhu uyu ni wabwino.” Wina adakamba, “Notho! Wanyenga wandhu.” 13Nambho padalibe mundhu uyo wadakamba ngani za Yesu pa ndhandala, ndande amaopa achogholeli wa Ayahudi.
14Pwando yapo lidafikila pakatikati, Yesu wadapita pa Nyumba ya Amnungu, ni kuyamba kuyaluza. 15Basi, Ayahudi adazizwa ni kukamba, “Mundhu uyu wapata kuti mayaluzo yaya niuku siwadasome?”
16Ndiipo Yesu wadayangha, “Mayaluzo yayo niyaluza opande yanga, nambho yachoka kwa yujha wanituma. 17Mundhu uyo wakonda kuchita icho afuna Amnungu, siwajhiwe mayaluzo yanga ngati yachokela kwa Amnungu, kapina nikamba yanga namwene. 18Mundhu wajhikambila mwene wafunafuna uelekelo wake mwene, nambho uyo wafunafuna uelekelo wa uyo wanituma, mmeneyo wazene ni walibe voipa mkati mwake. 19Bwanji Musa siwadakupacheni Thauko? Nambho palibe mmojhi wanu uyo waligwila thauko. Ndande mufuna kunipha?”
20Ndiipo wandhu adamuyangha, “Iwe uli ni viwanda! Yani wafuna kukupha?”
21Yesu wadaayangha, “Ine nachita chizindikilo chimojhi, mwaonjhe chakudabwichani 22Musa wadakuagizani mwachite mdulidwe wana wanu. Ingakhale silidachoke kwa Musa, nambho lidachokela kwa azee wanu. Namwe mumchita mundhu mdulidwe mbaka Siku lo Pumulila. 23Ingakhale mundhu wachitidwa mdulidwe mbaka Siku Lopumulila dala Thauko silida wanangidwa, ndande yanjhi mukwiya ndande ine namlamicha mundhu Siku Lopumulila? 24Msidamlamula mundhu kwa kumpenya kubwalope, nambho mchoche lamulo lovomelezeka.”
Bwanji, yuno nde Kilisito?
25Wandhu wina a ku Yelusalemu adamatofunjhana, “Bwanji, mundhu yujha amfunafuna amphe sinde uyu? 26Chipano wali pano, wakamba pachogolo pa wandhu wonjhe, nambho palibe uyo wamkambila kandhu. Bwanji, kapina achogholeli ajhiwa kuti uyu nde Kilisito? 27Nambho kilisito yapo siwajhe palibe mundhu uyo siwamjhiwe kumalo uko wachoka, nambho ife tijhiwa uko wachoka mundhu uyu!”
28Ndiipo, Yesu yapo wamayaluza pa Nyumba ya Amnungu wadakweza mvekelo ni kukamba, “Anyiimwe munijhiwa ni mujhiwa uko nichoka. Sinidajhe kwa lamulo langa namwene, nambho uyo wanituma ine wazene, namwe simumjhiwa. 29Nambho ine nimjhiwa ndande nachoka kwake, nde uyo wanituma.”
30Ndiipo, wandhu amafuna kumgwila, nambho palibe uyo wadayesa kumgwila ndande ndhawi yake idali ikali yosafike. 31Wandhu ambili pagulu lijha adamkhulupilila, adakamba, “Bwanji, Kilisito yapo siwajhe siwachite vizindikilo vavikulu kupitilila ivi wachita mundhu uyu?”
Alonda adatumidwa amgwile Yesu
32Afalisayo adavela wandhu niang'olong'ota kuusu nghani za Yesu. Ndiipo anyiiwo ni ajhukulu wakulu wadaatuma alonda amgwile. 33Chimwecho Yesu wadaakambila, “Nikali namwe kwa ndhawi yo chepa, ndiipo sinipite kwa yujha wanituma. 34Simunifunefune nambho simuniona, ni yapo sinikhale ine anyimwe simkhoza kufika.”
35Achogoleli wa Ayahudi adakambilana achinawene kwa chinawene, “Mundhu uyu siwapite kuti uko sitikhoza kumfunafuna? Siwapite kwa Ayahudi yawo ali kwa Agiliki, ni kwaayaluza? 36Wali ni mate yanji yapo wakamba simunifunefune nambho simunipheza, ni simukhoza kufika?”
Viwila va majhi ya umoyo
37Pasiku lothela siku la phwando, Yesu wadaima, wadakamba kwa mvekelo waukulu, “Uyo wali ni lujho wajhe kwanga wamwe. 38Ngati umo yakambila Malembo Yoyela, ‘Uyo wanikhulupilila ine, viwila va majhi ya umoyo sivisililike mumtima mwake!’” 39Wadakamba chimwecho kuusu Mzimu Woyela uwo samlandile anyiyawo amkhulupilila. Ndhawi imeneyo Mzimu Woyela udali ukali siudafike ndande Yesu wadali wakali osapachidwe ulemelelo.
Mkangano pakati pa wandhu kuusu Yesu
40Wandhu wina pa gulu lijha yapo adavela nghani za Yesu, adakamba, “Zenedi mundhu uyu nde yujha mlosi!”
41Wina adakamba, “Uyu nde Kilisito!”
Nambho wina adakamba kuti, “Siikhozeke bwanji Kilisito wachokele ku Galilaya? 42Bwanji malembo Yoyela siyakamba kuti, Kilisito siwachokele kukhamu la Daudi, ni siwabadwe ku Beselehemu, mujhi wa Daudi?” 43Ndiipo kudachokela mkangano pakati pa gulu la wandhu ndande ya Yesu. 44Wandhu wina amafuna kumgwila nambho padalibe uyo wadayesa kumgwila.
Achogholeli wa Ayahudi akana kumkhulupilila Yesu
45Chimwecho alonda adabwela kwa ajhukulu wakulu ni Afalisayo, ni anyiiwo adaafunjha, “Ndande yanji simudajhenaye pano?”
46Alonda adayangha, “Palibe mundhu wakhoza kukamba ngati umo wakambila mundhu uyu!”
47Ndiipo, Afalisayo adaafunjha wajha alonda, “Bwanji namwe mwanyengeka? 48Palibe mchogholeli waliyonjhe kapina Afalisayo uyo wamkhulupilila? 49Nambho gulu ili la wandhu lidamkhulupilila uku lali silijhiwa Thauko la Musa, gulu limenelo lalesedwa ni Amnungu!”
50Ndiipo Nikodemo mmojhi wa Afalisayo, uyo wadamchata Yesu usiku, wadafunjha, 51“Bwanji Thauko lathu limlamula mundhu wakali osavecheledwe huti ni kujhiwa wachita chiyani?”
52Nawo adayangha, “Nawenjho wachoka ku Galilaya? Yapenyecheche malembo yoyela, pamenepo nde siujhiwe ku Galilaya siwachoka mlosi!” 53Ndiipo, onjhe adachoka, kila mmojhi wadabwela kukhomo lake.

ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖

Yohana 7: NTNYBL2025

គំនូស​ចំណាំ

ចែក​រំលែក

ចម្លង

None

ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល