Yohana 10
10
Chifani cha owesa
1Yesu wadakamba, “Zenedi nikukambilani, waliyonjhe uyo siwalowa mkhola la mbelele kopitila pachicheko, nambho wakwela ni kulowela pamalo pina, mmeneyo mnghungu ni olanda. 2Nambho uyo walowa koopitila chicheko chimecho, mmeneyo nde owesa wa mbelele. 3Mlonda wachakulila, ni mbelele zivela mvekelo wake, nayo wazitana mbelele kila imojhi kwajhina lake, ni kuzitulucha kubwalo. 4Ndiipo wakatho zitulucha kubwalo wazichogolela mbelele, nazo zimchota, ndande ziujhiwa mvekelo wake. 5Mbelele zimenezo sizikhoza kumchata mlendo, nambho sizimthawe ndande sizijhiwa mvekelo wake.”
6Yesu wakambila chifani ichi, nambho anyiiwo siadajhiwe icho wamakambila.
Yesu Owesa wa Bwino
7Ndiipo wadakambilanjho, “Zene ni ikukambilani, ine ni chicheko cha mbelele. 8Onjhe anyiyao adanichogolela anghungu ni olanda, ni mbelele sizidavechele. 9Ine ni chicheko. Mundhu waliyonjhe uyo siwalowe kupila ine siwaomboke, siwalowe ni kutuluka, ni kupheza dyela. 10Mnghungu wakujha kuti wabe, kupha ni kuwananga. Ine nidajha kuti mukhale ni umoyo wa muyaya chimwecho akhale nawo siku zonjhe.”
11“Ine owesa wabwino. Owesa wabwino wachocha umoyo wake ndande ya mbelele zake. 12Owesa wa mkokolo, ni mbelele osati zake, yapo waona mibinji, wazisiya mbelele ni kuthawa, chimwecho mibinji izigwila ni kuzisiyanicha. 13Iye wathawa ndande ni owesa wa mkokolo, iye siwasamala mbelele. 14Ine ni owesa wabwino. Nizijhiwa mbelele izo zili zanga, ni mbelele zanga zinijhiwa ine, 15ngati Atate umo anijhiwila ine, nane umo najhiwila Atate. Niuchocha umoyo wanga ndande ya anyiiwo. 16Ni nili ni mbelele zina palibepo mkhola umu. Ifunika nijhenawo, nawo savele mvekelo wanga, ni sikukhalepo ni gulu limojhi ni owesa mmojhi.”
17“Ndande iyi, Atate anikonda ni kuuchocha umoyo wanga kuti niulandilenjho. 18Palibe uyo wanilanda umoyo wanga, ine niuchocha namwene. Nikhoza kuuchocha ni nikhoza kuutenganjho. Nde umo Atate anilamulila nichite.”
19Kudali ni kulimbananjho pakati pa Ayahudi ndande ya mawu yayo wamayakamba Yesu. 20Ambili pakati pao adakamba, “Wali ni viwanda, ni opande njelu! Ndande yanji timvechele?”
21Wina adakamba, “Mawu yaya osati ya mundhu wa viwanda. Bwanji mundhu wa chiwanda wakhoza kulamicha maso ya mundhu siwapenya?”
Yesu wakanidwa ni Ayahudi
22Ndhawi imeneyo idali ndhawi yozizila, ndiipo kudalipo ni phwando la kuielechanjho nyumba ya Amnungu ku Yelusalemu. 23Yesu nayo wamatoenda mu nyumba ya Mnungu mu msasa wa Solomoni. 24Chimwecho gulu la wandhu lidamzungulila, lidamfunjha, “Siutiike mmaganizo mbaka siku lanji? Ngati iwe nde Kilisito, tikambile padanga.”
25Yesu wadayangha, “Nakukambilani nambho simuvomela. Njhito izo nichita kwa ulamuli wa Atate wanga linichochela umboni. 26Anyiimwe simukhulupilila ndande anyiimwe osati mbelele zanga. 27Ngati mujha mbelele zivela mvekelo wa owesa wao, wandhu wanga achijhiwa icho nichikamba nane najhiwa ni akhala ochatila wanga. 28Ine napacha umoyo wamuyaya ni muyaya siasiana ni Amnungu. 29Atate wanga yao anipacha mbelele zimenezo niwakulu kupitilila onjhe, palibe uyo wakhoza kuzichocha kwa Atate wanga. 30Ine ni Atate wanga tili amojhi.”
31Ndiipo Ayahudi adatondolanjho miyala kuti amponye Yesu. 32Yesu wadaakambila, “Nakulangizani njhito zambili kuchoka kwa Atate. Njhito iti pa zimenezo ikuchitani munibule miyala?”
33Ayahudi adamuyangha, “Sitikuponya miyala ndande ya njhito za bwino, nambho ndande ya kwaatukwana Amnungu! Mate yake ujhichita iwe Amnungu, ni iwe ni mundhupe.”
34Ndiipo Yesu wadaayangha, “Bwanji, siidalembedwe mu malembo, kuti, ‘Ine nakamba anyiimwe ni minungu?’ 35Ikhakala Amnungu wadaatana minungu wajha adapachidwa mawu la Amnungu, chimwecho malembo ya Amnungu ni ya uzene siku zonjhe. 36Bwanji anyiimwe mkamba kuti nitukwana ndande nikamba ine ni mwana wa Amnungu? Ine Atate adanisangha ni kunituma pa jhiko la panjhi. 37Ngati sinichita njhito iyo natumidwa ni Atate, simdanikhulupilila. 38Nambho ngati nizichita njhito za Atate, atangati simunikhulupilila, zikhulupilileni njhito zimenezo, kuti mwajhiwe Atate ali mkati mwanga, nane nili mkati mwao.”
39Adaesanjho kumgwila nambho wadapulumuka mmanja mwao.
40Ndiipo Yesu wadapitanjho ku chija la mchinje Yolodani, pamalo yapo wamabatizila Yohana, wadakhala kumeneko. 41Wandhu ambili adamchata adakamba, “Yohana siwadachite chizindikilo chilichonjhe. Nambho yonjhe yayo wayakamba Yohana kuusu mundhu uyu yazene.” 42Wandhu ambili adamkhulupilila Yesu pamalo pamenepo.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Yohana 10: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង

ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.