Yohana 1
1
Mawu wadachitika thupi
1Poyamba wadalipo Mawu, nayo wadali ni Amnungu nayo wadali Mnungu. 2Kuyambila mmayambo Mawu wadali ni Amnungu. 3Kupitila iye vindhu vonjhe vidaumbidwa, palibe icho chida umbidwa popande iye. 4Iye wadali chiyambo cha umoyo ni umoyo umenewo udali dangalila kwa wandhu. 5Dangalila limenelo liwala mumdima, ni mdima siudalikhoze kulithima dangalila limenelo kuti lisawale.
6Amnungu wadamtuma mundhu mmojhi jhina lake Yohana, 7uyo wadajha ngati mmboni, kuti walichitile umboni dangalila limenelo kupitila iye wandhu wonjhe akhoze kukhulupilila. 8Yohana siwadali dangalila mmeneyo, wadajhape kwakambila wandhu nghani za dangalila limenelo. 9Ili nde lidali dangalila la zene, dangalila ilo likujha pajhiko ni kwawalila wandhu wonjhe.
10Ndiipo Mawu wadali pajhiko, kwakupitila iye jhiko lidaumbidwa, nambho jhiko silimamjhiwe. 11Wadajha mujhiko lake mwene, nambho akwake siada mlandile. 12Nambho anyiyawo adamlandila, nikumkhulupilila mwadapacha nghongono za kukhala wana Amnungu, nde anyiwajha alikhulupilila jhina lawo, 13anyiyawo abadwa asati kwa mwazi, kapina kwa kukonda kwa thupi au kukonda kwa mundhu, nambho Amnungu nde yawo adali Atate wao.
14Mawu nalo lidakhala mundhu, ni wadakhala kwathu. Nafe tauona ulemelelo wake, ulemelelo wa Mwana wa yokha wa Atate, wajhala ubwino ni uzene.
15Yohana wadakambila wandhu nghani za mmeneyo, wadakamba kwa mvekelo, “Uyu nde yujha timamchochela umboni kwakukamba chimwechi, ‘Siwajhe mundhu mmojhi uyo wali wamkulu kusiyana niine, mateyake wadalipo ine nikali osabadwe.’ ”
16Kwakupitila ukwanilicho wake ife tapata ubwino uwo upitilila ubwino woyamba. 17Pakuti Amnungu wadachocha thauko kwakupitila Musa, nambho ubwino ni uzene vidajha kwa kupitila Yesu Kilisito. 18Palibe uyo waonapo Amnungu muyaya. Nambho Mwana wao wapayokha uyo walunjana ni Atate, nde uyo wati jhiwicha nghani za Amnungu.
Utenga wa Yohana Mbatizi
Matayo 3:1-12; Maluko 1:1-8; Luka 3:1-18
19Uno nde umboni wa Yohana uwo wadauchocha ndhawi iyo achogholeli a Chiyahudi ku Yelusalemu, yapo wadatuma Alawi ni ajhukulu, amfunjhe kuti “Iwe yani?”
20Yohana siwadakane kwaakambila uzene, popande kubisa, kuti, “Ine osati Kilisito.”
21Ndipo adamfunjha, “Chipano iwe yani? Bwanji, iwe Elia?”
Yohana wadayangha, “Osati ine.”
Ndipo adamfunjhanjho, “Bwanji iwe nde yujha mlosi?”
Yohana wadakana, “Notho!”
22Anyiiwo adamfunjha, “Iwe yani? Tikambile, tikaapache yangho yawo atituma.”
23Yohana wadayangha, “Ine nde yujha uyo mlosi Isaya wadakamba nghani zanga,
‘Mvekelo wa mundhu utana kuphululu.
Konjani njila ya Ambuye.’ ”
24Wandhu anyamenewo adatumidwa ni Afalisayo. 25Ndiipo, adamfunjha Yohana, “Ngati iwe osati Masiya, kapina Eliya, kapina yujha mlosi, ndande yanji chipano ubatiza?”
26Yohana wadayangha, “Ine nibatiza kwa majhi, nambho walipo mmojhi, pakati panu, uyo mukali osamjhiwe. 27Siwajhe pa mbuyo pa ine. Nambho sinikhoza kumasula luzi la malapasi yake.”
28Vindhu vimenevo vidachitika ku Besania, mchija la mchinje Yoludani uko Yohana wamabatizila wandhu.
Mwana wa Mbelele wa Amnungu
29Mawa lake, Yohana wadamuona Yesu ni wajha kwaiye, wadakamba, “Yuno nde Mwana wa Mbelele wa Amnungu uyo wachocha chimo la wandhu! 30Uyu nde uyo nimafotokoza nghani zake kuti, ‘Pambuyo panga siwajhe mundhu mmojhi uyo wali wamkulu kupunda kupitilila ine, pakuti wadalipo ine nikali osabadwe.’ 31Ine namwene sinimamjhiwe, nambho ni batiza kwa majhi kuti wandhu Aizilaeli amjhiwe.”
32Yohana wadachitila umboni chimwechi, “Ni adauona Mzimu niuchika ngati nghunda kuchoka kumwamba ni kutula pa mwamba pake. 33Ine sinimamjhiwe, nambho uyo wanituma kubatiza wandhu kwa majhi wanikambila, ‘Mundhu uyo siwauone mzimu niuchika kuchoka kumwamba ni kukhala pa mwamba pake, nde uyo wabatiza kwa Mzimu Woyela.’ 34Ine naona nikuchitila umboni kuti uyu nde Mwana wa Amnungu.”
Oyaluzidwa oyamba a Yesu
35Mawa lake, Yohana wadaimanjho pajha pamojhi ni oyaluzidwa wake awili. 36Yapo wadamuona Yesu niwapita, wadakamba, “Penyani! Uyu nde Mwana wa Mbelele wa Amnungu.”
37Anyiwajha oyaluzidwa yapo adamvela Yohana ni wakamba mawu yameneyo, adamchata Yesu. 38Ndiipo, Yesu wadang'anamuka, ni yapo wadaona oyaluzidwa achameneo niamchata, wadafunjha, “Mfunafuna chiyani?”
Anyiiwo adamuyangha, “Oyaluza, mukhala kuti?”
39Yesu wadatana, “Majhani, namwe simunione.” Chimwecho adamchata, ni kupaona pamalo yapo wamakhala, adalongeza naye siku limenelo.
40Andulea mbale wa Simoni Petulo, wadali mmojhi wa wandhu awili anyiyawo adamvela Yohana niwakamba chimwecho, adamchota Yesu. 41Pampajha icho wadachita Andulea, wadapezana ni mbale wake, Simoni, wadamkambila, “Tamuona Mesiya” Mateyake Kilisito. 42Ndiipo, wadampeleka Simoni kwa Yesu.
Chimwecho Yesu wadampenya Simoni nikukamba, “Iwe ni mwana wa Yohana. Chipano siutanidwe Kefa” Pamkambo wa Chighiliki Petulo, mateyake, mwala.
Yesu waatana Filipo ni Nasanaeli
43Mawa lake, Yesu wadalamula kupita kumujhi wa Galilaya, kumeneko wadampheza Filipo, wadamkambila “Nichate.” 44Filipo wadali mundhu wa kumujhi wa Betisaida, mujhi uwo Petulo ni Andulea amakhala. 45Filipo yapo wadampheza Nasanaeli, wadamkambila, “Tampheza uyo Musa wadalemba nghani zake muchikalakala cha Thauko, ni uyo alosi adalemba nghani zake, ndekuti Yesu mwana wa Yusufu wa ku Nazaleti.”
46Nasanaeli nayonjho wadamfunjha Filipo, “Bwanji, chindhu cha bwino chikhoza kuchokela ku Nazaleti?”
Ndiipo Filipo wadayangha, “Majha uone.”
47Yesu yapo wadamuona Nasanaeli niwajha kwake, wadakamba nghani zake, “Mmeneyo Muizilaeli mwene. Palibe choipa mkati mwake.”
48Nasanaeli nayonjho wadamfunjha, “Waniona bwanji?”
Yesu wadayangha, “Yapo udali panjhi pa mtengo wa mtini, Filipo wakali osakutane, nidakuona.”
49Ndiipo Nasanaeli wadamkambila, “Oyaluza, imwe ni Mwana wa Amnungu. Imwe ni Amfumu a ku Izilaeli!”
50Ndiipo Yesu wadafunjha, “Wakhulupilila ndande nakukambila kuti nakuona panjhi pa mtengo wa Mtini? Siuvione vindhu vavikulu kupunda kupitilila ivi.” 51Yesu wadaendekela kukamba, “Nikukambilani uzene, simuone kumwamba nikuvunukuka niatumiki akumwamba Amnungu ni akwela ni kuchika pamwamba pa Mwana wa Amnungu.”
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Yohana 1: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង

ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.