Vichito 3
3
Petulo wamlamicha mundhu wa ndendele
1Siku limojhi Petulo ni Yohana amapita ku Nyumba ya Mnungu kupembhela ndhawi ya saa tisa usana. 2Ndiipo kudali mundhu mmojhi uyo wandendele kuyambila kubadwa kwake. Kila siku wamatengedwa ni kuikidwa pakhomo la Nyumba ya Mnungu ilo limatanidwa, Khomo Labwino, kuti wajhipembha ndalama kwa wandhu yawo amalowa ni kutuluka Mnyumba ya Mnungu. 3Mundhu mmeneyo yapo wadaaona Petulo ni Yohana naalowa pa nyumba ya Mnungu, wadaapembha ampache ndalama. 4Petulo ni Yohana adampenyechecha mundhu yujha, ndiipo Petulo wadamkambila, “Tipenye ife.” 5Mundhu yujha wadaapenya niwalindilila kupata kandhu kuchokela kwa anyiiwo. 6Nambho Petulo wadamkambila, “Nilibe ndalama, nambho nikupacha chindhu icho nilinacho. Mu jhina la Yesu wa ku Nazaleti ima ni ujhiyenda.” 7Ndiipo Petulo wadamgwila yujha mundhu kwa jhanja lake lakwene ni kumuimicha, ndhawi imweyo myendo yake ni vifundo va myendo yake vidali ni mbhavu. 8Wadalumbha ni kuima ni kuyamaba kuyenda. Ndiipo wadalowa pa Nyumba ya Mnungu pamojhi ni Petulo ni Yohana, niwayenda ni kuyamika ni kumtamanda Mnungu. 9Wandhu yawo adali pajha adamuona iye niwayenda ni kumtamanda Mnungu. 10Yapo adamjhiwa kuti nde yujha wamakhala pakhomo la Nyumba ya Mnungu ilo litanidwa, Khomo Labwino, ni kupembha ndalama, adazizwa kupunda ni sadajhiwe icho chimayendekela.
Petulo walalikila pa Nyumba ya Mnungu
11Mundhu yujha wadalamichidwa yapo wamachogozana ni Petulo ni Yohana. Wandhu wonjhe adadabwa kupunda, adaathamangila mbaka kumalo kumatanidwa pa khumbi la Solomoni. 12Ndiipo Petulo yapo wadaona kuti wandhu asonghana, wadaakambila, “Anyiimwe wandhu a ku Izilaeli, ndande yanji muvizizwa vindhu ivi? Bwanji mutipenyechecha kwa kutizizwa ngati ife tamchita mundhu uyu wayende kwa mbhavu zathu, kapina ndande ife abwino pachogolo pa Amnungu? 13Mnungu wa Atate wathu Ibulahimu ni Isaka ni Yakobo, wadamuhyucha Yesu Mbuye wathu. Nambho anyiimwe mudampeleka kwa akulu a maulamulilo ni kumukana pamaso pa Pilato, ingakhale Pilato wadafuna kumsiilila Yesu. 14Anyiimwe mudamkana Yesu, mundhu yujha Woyela ni wovomelezeka pamaso pa Mnungu, mdampembha Pilato wamasulidwe wakupha yujha. 15Ndiipo mudampha mundhu uyo wadali chiyambo cha umoyo, nambho Mnungu wadamuhyukicha. Ife ni mboni ni tifotokoza ivo vidachokela. 16Kwa kulikhulupilila jhina la Yesu, mundhu uyu mumuona ni kumjhiwa wapachidwa mbhavu. Chikhupililo cha Yesu nde icho chamlamichilatu mundhu uyu, ngati umo mumuonela mwaonjhe.”
17“Chipano achabale wanga, nijhiwa kuti anyiimwe mudachita popande kujhiwa ngati umo adachitila achogoleli wanu. 18Nambho kwa kupitila yaya Mnungu wadakwanilicha chijha wadalosa kupitila alosi wake wonjhe, kuti Kilisito siwapachikidwe. 19Chimwecho lapani, mumbwelele Mnungu, kuti wakulekeleni machimo yanu. 20Mkachita chimwecho, simchuluchidwe mbhavu za Mzimu Woyela kuchokela kwa Ambuye, nawo samtume Yesu Kilisito uyo amsangha, 21uyo wamafunika kulandilidwa kumwamba mbaka ijhe ndhawi yochita kila kandhu chikhale cha chipano. Nghani izi zimakambidwa ni Mnungu kupitila alosi wake woyela kuyambila chiyambo cha jhiko la panjhi. 22Chimchijha, Musa wadakamba, ‘Ambuye Mnungu wanu siwakupacheni mlosi uyo siwachokele pakati panu. Namwe mufunika kumvechela mmeneyo kwa kila chindhu icho siwakukambileni. 23Mundhu waliyonjhe uyo siwamuvela mlosi mmeneyo, siwapatulidwe kuchokela kwa wandhu a Mnungu ni kuphedwa.’ 24Yetu, alosi wonjhe kuyambila Samweli ni wajha adachata, wonjhe adalosela kuhusu nyengo zino. 25Yajha adayakamba Amnungu kwa njila ya alosi ndande yanu, ni anyiimwe muli muyameneyo adayakamba Amnungu ni azee wanu, ngati umo wamkambila Ibulahimu, ‘Kwanjila ya mbadwa wako wandhu wonjhe apajhiko sapachidwe mwawi.’ 26Ndiipo Amnungu adamuhyukicha uti mtumuki wake ni kumtuma kwa anyiimwe, kuti wakupacheni mwawi kwa kukuchitani kila mmojhi wanu wasiye vichito vake voipa.”
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 3: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.