Vichito 26
26
Poolo wajhiteteza pachogolo pa Mfumu Agilipa
1Agilipa wadamkambila Poolo, “Ukhoza chipano kujhiteteza umwene wake.” Poolo wadakweza jhanja lake kulangiza kuti amvecheche, wadayamba kujhiteteza wadakamba,
2“Mfumu Agilipa, nijhiona kuti nili mwawi lelo lino kuima pachogolo panu ni kujhiteteza nghani za milandu yonjhe iyo anipelekela Ayahudi, 3hasa ndande, imwe muujhiwa bwino mthethe wonjhe wa Ayahudi ni vindhu ivo nichuchana nawo, chimwecho nipembha univechele kwa kulimba mtima.”
4Ayahudi wonjhe ajhiwa umo nimakhalila kuyambila nikali wamng'ono. Kuyambila chiyambo cha umoyo wanga, mujhiko langa ni yapo nidali ku Yelusalemu. 5Anyiiwo anijhiwa kuyambila kwa ndhawi ya itali, ni akhoza kunifotokozela yameneyo ngati akafuna, kuyambila ndhawi ya itali nidali mmojhi wa gulu la Afalisayo ilo ligwila thauko la dini ya chiyahudi kupitilila gulu lalilonjhe. 6Nanenjho chipano ndande ya chikhulupililo changa, lelo nipachidwa mlandu kwa chijha Mnungu wadaahidi achatate wathu. 7Ahadi iyo nde iyo mafuko yathu khumi ni yawili akhulupilila kuiona niikwanilichidwa, uku niyamtumikila Mnungu kwa mtima wonjhe usiku ni usana. Imwe amfumu ndande ya yaya, Ayahudi anyiiawa anipacha mlandu. 8Ndande yanji waliyonjhe pakati panu waona kulimba kukhulupilila kuti Mnungu wakhoza kwaahyukicha wandhu yawo amwalila?
9“Ine nanenjho nidakhulupilila kuti, nifunika kuchita vindhu vambili ndande yo lichucha jhina la Yesu wa ku Nazaleti. 10Ndeumo nidachitila yapo nidali ku Yelusalemu. Ajhukulu waakulu adanipacha ulamulilo naagwile wandhu amlambila Mungu ni kwaika mndende. Niyapo amalamulidwa kupedwa ine nidabula gudugudu, lovomela kuti apedwe. 11Nidapita mu nyumba zao zokomanilana nidaalanga ni kwakakamiza kuti amtukwane Mnungu. Nidali ni mbhwayi ni wandhu achamenewo mbaka nidapita mmijhi ina kwaafunafuna kuti navutiche.”
Poolo wafotokoza umo wadamkhulupilila Kilisito
Vichito 9:1-19; 22:6-16
12“Siku limojhi yapo nidali paulendo wopita ku Damesiki uku nili mbhwayi, nidapachidwa ulamulilo kuchokela kwa ajhukulu wakulu. 13Olemekezeka, yapo nidali mnjila siku lilijha ndhawi ya saa sita usana, nidaona dangalila lalikulu kuchokela ku mwamba, ilo limawala kupitilila dangalila la jhuwa. Limawala kunizungulila ine pamojhi ni anyiwajha nidali nawo paulendo. 14Taonjhe tidagwa panjhi, nidavela mvekelo niukamba nane muchimkambo cha Chihebulaniya, ‘Saulo, Saulo, ndande yanji univuticha? Ujhipweteka umwenewake ndande ya kuchuchana nane, ngati punda umo wabulila mtawi mkwapulo wa Mbuye wake.’ 15Nidafunjha, ‘Imwe ayani, Ambuye?’ Ambuye adayangha, ‘Ine Yesu, uyo umvuticha. 16Nambho chipano ima, nakuchokela dala nikuchite mtumiki wanga, iwe siufotokeze nghani zanga ni siwafotokozele wandhu yayo wayaona lelo lino ni yayo sinikulangize pambuyo. 17Sinikulamiche kuchokela kwa Ayahudi anjhako ni wandhu osati Ayahudi, yawo nikutuma kwao. 18Kuti akhoze kunijhiwa ni achoke kumdima ni kupita mdangalila, achoke ku mbhavu za Satana ni kulowa muufumu wa Mnungu, dala akhoze kulekeleledwa machimo yao ni kupata malo, pakati pa wajha anikhulupilila.’”
Poolo wafotokoza njhito yake
19“Chimwecho, Mfumu Agilipa, ine sinidayakane masombhenya yadachoka kumwamba. 20Nidayamba kwaauzila wandhu aku Damesiki ni Yelusalemu ni malo ya Yudea pamojhi ni wandhu osati Ayahudi. Nidaakambila kuti alape machimo yawo ni kumbwelela Mnungu, nialangiza kwa vichito vao kuti alapa. 21Kwa ndande imeneyo, Ayahudi adanigwila yapo nidali mu nyumba ya Mnungu, ni amafuna kunipha. 22Nambho Mnungu wadanisunga mbaka lelo lino nili wamoyo. Chimwecho niima pano uku naakambila wakulu akulu ni wang'ono yajha nayavela ni kuyaona, sinikamba yambili nambho chijha chidakambidwa ni Musa ni alosi wa Mnungu, 23kuti Kilisito sivutichidwe, ni iye nde siwakhale woyamba kuhyuka payojhe yawo amwalila. Siwawalile dangalila la uwomboli kwa wandhu wake ni wandhu osati Ayahudi.”
24Yapo Poolo wamajhiteteza chimwechi, Fesitasi wadakamba kwa mvekelo, “Iwe Poolo, wazungulila njelu kani! Kusoma kupunda kwakuchita kuti ukhale wamisala!”
25Poolo wadayangha, “Ine osati wamisala, Olemekezeka Fesitasi! Nambho icho nachikamba ni cha uzene ni chili ni mate. 26Amfumu Agilipa ajhiwa bwino vindhu ivi, chipano nikhoza kukamba popande mandha pachogolo panu. Sinikaikila kuti vindhu ivi avijhiwa, ndande palibe icho chitachitika ko jhibisa. 27Mfumu Agilipa bwanji, mwaakhulupilila alosi? Nijhiwa kuti muyakhulupilila.”
28Mfumu Agilipa adamfujha Poolo, “Uganiza ukhoza kuninyengelela kwa ndhawi yochepa kuti nikhale Mukilisito?”
29Poolo wadayangha, “Ata ngati ikhale ndhawi yochepa kapina yaitali, nipembhela kwa Mnungu kuti iwe pamojhi ni wandhu wonjhe anivechela lelo, aomboledwe ili akhale ngati ine, nambho sadamangidwaa maunyolo ngati ine!”
30Pambuyo pa kukamba yameneyo, Mfumu Agilipa ni Fesito wamkulu wa ku Yudea ni Belinike ni wajha wonjhe adali pamojhi nawo kwa pamojhi adaima. 31Ndiipo adatuluka mkati. Anyiiwo amakambilana achinawene, niakamba, “Mundhu uyu siwadalakwe chilichonjhe icho wafunika mbaka waphedwe kapina kuikidwa mu ndende.” 32Ndiipo Agilipa wadamkambila Fesito, “Mundhu uyu wadakasiililidwa, ngati siwadakapeleka mlandu wake kwa Mfumu wa ku Loma.”
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 26: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Vichito 26
26
Poolo wajhiteteza pachogolo pa Mfumu Agilipa
1Agilipa wadamkambila Poolo, “Ukhoza chipano kujhiteteza umwene wake.” Poolo wadakweza jhanja lake kulangiza kuti amvecheche, wadayamba kujhiteteza wadakamba,
2“Mfumu Agilipa, nijhiona kuti nili mwawi lelo lino kuima pachogolo panu ni kujhiteteza nghani za milandu yonjhe iyo anipelekela Ayahudi, 3hasa ndande, imwe muujhiwa bwino mthethe wonjhe wa Ayahudi ni vindhu ivo nichuchana nawo, chimwecho nipembha univechele kwa kulimba mtima.”
4Ayahudi wonjhe ajhiwa umo nimakhalila kuyambila nikali wamng'ono. Kuyambila chiyambo cha umoyo wanga, mujhiko langa ni yapo nidali ku Yelusalemu. 5Anyiiwo anijhiwa kuyambila kwa ndhawi ya itali, ni akhoza kunifotokozela yameneyo ngati akafuna, kuyambila ndhawi ya itali nidali mmojhi wa gulu la Afalisayo ilo ligwila thauko la dini ya chiyahudi kupitilila gulu lalilonjhe. 6Nanenjho chipano ndande ya chikhulupililo changa, lelo nipachidwa mlandu kwa chijha Mnungu wadaahidi achatate wathu. 7Ahadi iyo nde iyo mafuko yathu khumi ni yawili akhulupilila kuiona niikwanilichidwa, uku niyamtumikila Mnungu kwa mtima wonjhe usiku ni usana. Imwe amfumu ndande ya yaya, Ayahudi anyiiawa anipacha mlandu. 8Ndande yanji waliyonjhe pakati panu waona kulimba kukhulupilila kuti Mnungu wakhoza kwaahyukicha wandhu yawo amwalila?
9“Ine nanenjho nidakhulupilila kuti, nifunika kuchita vindhu vambili ndande yo lichucha jhina la Yesu wa ku Nazaleti. 10Ndeumo nidachitila yapo nidali ku Yelusalemu. Ajhukulu waakulu adanipacha ulamulilo naagwile wandhu amlambila Mungu ni kwaika mndende. Niyapo amalamulidwa kupedwa ine nidabula gudugudu, lovomela kuti apedwe. 11Nidapita mu nyumba zao zokomanilana nidaalanga ni kwakakamiza kuti amtukwane Mnungu. Nidali ni mbhwayi ni wandhu achamenewo mbaka nidapita mmijhi ina kwaafunafuna kuti navutiche.”
Poolo wafotokoza umo wadamkhulupilila Kilisito
Vichito 9:1-19; 22:6-16
12“Siku limojhi yapo nidali paulendo wopita ku Damesiki uku nili mbhwayi, nidapachidwa ulamulilo kuchokela kwa ajhukulu wakulu. 13Olemekezeka, yapo nidali mnjila siku lilijha ndhawi ya saa sita usana, nidaona dangalila lalikulu kuchokela ku mwamba, ilo limawala kupitilila dangalila la jhuwa. Limawala kunizungulila ine pamojhi ni anyiwajha nidali nawo paulendo. 14Taonjhe tidagwa panjhi, nidavela mvekelo niukamba nane muchimkambo cha Chihebulaniya, ‘Saulo, Saulo, ndande yanji univuticha? Ujhipweteka umwenewake ndande ya kuchuchana nane, ngati punda umo wabulila mtawi mkwapulo wa Mbuye wake.’ 15Nidafunjha, ‘Imwe ayani, Ambuye?’ Ambuye adayangha, ‘Ine Yesu, uyo umvuticha. 16Nambho chipano ima, nakuchokela dala nikuchite mtumiki wanga, iwe siufotokeze nghani zanga ni siwafotokozele wandhu yayo wayaona lelo lino ni yayo sinikulangize pambuyo. 17Sinikulamiche kuchokela kwa Ayahudi anjhako ni wandhu osati Ayahudi, yawo nikutuma kwao. 18Kuti akhoze kunijhiwa ni achoke kumdima ni kupita mdangalila, achoke ku mbhavu za Satana ni kulowa muufumu wa Mnungu, dala akhoze kulekeleledwa machimo yao ni kupata malo, pakati pa wajha anikhulupilila.’”
Poolo wafotokoza njhito yake
19“Chimwecho, Mfumu Agilipa, ine sinidayakane masombhenya yadachoka kumwamba. 20Nidayamba kwaauzila wandhu aku Damesiki ni Yelusalemu ni malo ya Yudea pamojhi ni wandhu osati Ayahudi. Nidaakambila kuti alape machimo yawo ni kumbwelela Mnungu, nialangiza kwa vichito vao kuti alapa. 21Kwa ndande imeneyo, Ayahudi adanigwila yapo nidali mu nyumba ya Mnungu, ni amafuna kunipha. 22Nambho Mnungu wadanisunga mbaka lelo lino nili wamoyo. Chimwecho niima pano uku naakambila wakulu akulu ni wang'ono yajha nayavela ni kuyaona, sinikamba yambili nambho chijha chidakambidwa ni Musa ni alosi wa Mnungu, 23kuti Kilisito sivutichidwe, ni iye nde siwakhale woyamba kuhyuka payojhe yawo amwalila. Siwawalile dangalila la uwomboli kwa wandhu wake ni wandhu osati Ayahudi.”
24Yapo Poolo wamajhiteteza chimwechi, Fesitasi wadakamba kwa mvekelo, “Iwe Poolo, wazungulila njelu kani! Kusoma kupunda kwakuchita kuti ukhale wamisala!”
25Poolo wadayangha, “Ine osati wamisala, Olemekezeka Fesitasi! Nambho icho nachikamba ni cha uzene ni chili ni mate. 26Amfumu Agilipa ajhiwa bwino vindhu ivi, chipano nikhoza kukamba popande mandha pachogolo panu. Sinikaikila kuti vindhu ivi avijhiwa, ndande palibe icho chitachitika ko jhibisa. 27Mfumu Agilipa bwanji, mwaakhulupilila alosi? Nijhiwa kuti muyakhulupilila.”
28Mfumu Agilipa adamfujha Poolo, “Uganiza ukhoza kuninyengelela kwa ndhawi yochepa kuti nikhale Mukilisito?”
29Poolo wadayangha, “Ata ngati ikhale ndhawi yochepa kapina yaitali, nipembhela kwa Mnungu kuti iwe pamojhi ni wandhu wonjhe anivechela lelo, aomboledwe ili akhale ngati ine, nambho sadamangidwaa maunyolo ngati ine!”
30Pambuyo pa kukamba yameneyo, Mfumu Agilipa ni Fesito wamkulu wa ku Yudea ni Belinike ni wajha wonjhe adali pamojhi nawo kwa pamojhi adaima. 31Ndiipo adatuluka mkati. Anyiiwo amakambilana achinawene, niakamba, “Mundhu uyu siwadalakwe chilichonjhe icho wafunika mbaka waphedwe kapina kuikidwa mu ndende.” 32Ndiipo Agilipa wadamkambila Fesito, “Mundhu uyu wadakasiililidwa, ngati siwadakapeleka mlandu wake kwa Mfumu wa ku Loma.”
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
:
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.