Alom 1
1
1Ine Poolo, Mtumiki wa Yesu Kilisito ni mtumwi nasanghidwa ni kutanidwa ndande ya uthenga wa bwino wa Mnungu.
2Kalepo Mnungu wadaakambila wandhu kuti siwapache Uthenga uwu wabwino, kwa njila ya alosi wake mmalembo ya Mnungu. 3Nghani iyi yabwino imuusu mwana wa Mnungu Yesu kilisito, Mbuye wathu uyo wadabadwa ngati umo wandhu abadwila wadali wa khamu la Daudi, 4ni uyo kwa mbhavu za mzimu woyela, wadamjhiwicha kuti iye ni Mwana wa Mnungu ni kwa kuhyuka kwake, yani Yesu kilisito Mbuye wathu. 5Kwakupitila Yesu Kilisito, ine napachidwa ubwino wokhala mtumiki, ni kwandande yaiye nichogoze wandhu amayiko yonjhe kuti akhoze kukhulupilila ni kuvela Uthenga wa Bwino. 6Anyiimwe Aloma namwe ni amojhi mwa wandhu anyiyawo, mwatanidwa kuti mkhale wandhu wake kilisito mwene.
7Chipano, nikulembelani anyiimwe mwaonjhe muli Ku Loma, anyiimwe Mnungu wakukondani kupunda ni wadakusanghani mkhale wandhu wake mwene,
Nikupembhelani kwa Amnungu Tate wathu mkhale ni ubwino ni mtendele,
Kwaayamika Amnungu
8Poyamba, nimyamika Mnungu wanga kupitila Yesu kilisito ndande yanu mwaonjhe, pakuti kukhulupilila kwanu kuveka pa jhiko lonjhe. 9Mnungu uyo nimtumikila kwa mtima wanga wonjhe, pakuuzila uthenga wa mwana wake, nimmboni wanga kwa umo nikukumbukilani masiku yonjhe mmapembhelo yanga. 10Nimpembha Mnungu wakakonda wanipache malo ya bwino ya kujha kwaanyiimwe chipano. 11Pakuti nikhumbila kupunda kukuonani, kuti nikhoze kukutangatilani kupata mbhaso ya mzimu Woyela ya kukulimbichani chikhulupi chanu. 12Ndiipo anyiimwe pamojhi ni ine, titilane mtima kuti chikhulupi chatu chiime bwino.
13Achabale wanga, nifuna mjhiwe kuti nyengo zambili nidafuna kukuendelani, nambho mbaka sazino nachekelezedwa. Kuti nijhe kukutangatilani kwachita wandhu amkhulupilile Kilisito, ngati umo nidachitila kwa wandhu amayiko yina. 14Ine nifunika nilalikile Uthenga wa Bwino kwa wandhu yawo ali a Agiliki ni wandhu anyiawo osati Agiliki, asoma ni yawo sadasome. 15Ndendande nikumbila kupunda kulalikila uthenga wa bwino kwa anyiimwe muli ku mujhi wa Loma.
Mbhavu ya uthenga wa bwino
16Ine siniona njhoni kuuzila uthenga wa Bwino, wene ni mbhavu ya Mnungu, iyo yaombola wandhu wonjhe amkhulupilila Yesu. Kuyambila Ayahudi ni anyiawo osati ayahudi. 17Pakuti uthenga wa bwino walangiza umo Mnungu wafunila tikhale kuti tivomelezeke pachogolo pake, chindhu ichi chichitika kwa kumkhulupilila Yesu Kilisito, palibe china kupitilila chimecho, ngati umo yalembedwa mmalembo, “Mundhu wovomelezeka kwa Mnungu siwakhale kwa kumkhulupilila Mnungu.”
Kulakwa kwa wandhu
18Kuchokela kumwamba, Mnungu waakwiila wandhu wajha amkana ni achita voipa, anyiyawo kwa njila zao zoipa auchekeleza Uthenga wa Bwino kuti siudajhiwika. 19Vindhu vonjhe va Mnugu vili padanga kwa anyiiwo, ndande Mnungu mwene wadaviika padanga kwao. 20Kuyambila yapo Mnungu wadaumba jhiko, kukhoza kwake ni umnungu wake, ingakhale siuoneka kwa maso, wajhiwikana padanga. Wandhu akhoza kwajhiwa, kuchokana ni vindhu ivo waviumba ndande imeneyo palibe mundhu ata mmojhi wakhoza kukamba sitimjhiwa Mnungu. 21Ingakhale ajhiwa kuti kuli Mnungu, nambho sampacha ulemu uwo ufunika, ni samuyamika mmalo mwake maganizo yawo yali yoipa ni njelu zao zilibe kandhu ni zili ni usabwabwa. 22Achitadama kuti ali ni ekima, nambho ni asabwabwa. 23Asiya kumlambila Mnungu wa muyaya, ni pambuyo pake, avilambila viboliboli vili chifani cha mundhu uyo wamwalila, chifani cha zinyama, mbalami ni vokwawa.
24Ndande imeneyo, Mnungu wasiya achate khumbilo loipa la mitima yao, ni kuchitilana vindhu va njhoni achinawene kwa achinawene. 25Aung'anamula uzene wa Mnungu ni kuuchita ukhale unami, achilemekeza ni kuchilambila choumbidwa ni Mnungu pambuyo pa kumlambila Mnungu mwene, uyo idafukika kulambilildwa muyaya! Ikhale chimwecho.
26Chipano, Mnungu waasiya achate khumbilo loipa. Wachikazi ang'anamula matupi yawo, ni kutumila mosafunikile kwa kukhumbilana achinawene kwa achina wene. 27Ni wachimuna chimwecho, asiya kukhumbilana wamnuna ni wamkazi, akhumbilana anyiiwo kwa anyiiwo. Wachimuna achitilana vindhu va njhoni, chimwecho saalangidwe kuchokana ni vichito vao voipa.
28Pakuti wandhu adakana kumjhiwa Mnungu, Mnungu wasiya mumaganizo yao yoipa, achite vijha siadafunike kuvichita. 29Ajhala kila mtundu wa voipa, chigololo, kuipa, khumbilo loipa, maganizo yoipa. Ajhala njhanjhe, kupha ni ndewo, kunyenga ni ludyo la kukhala ni chuma, ni anyiiwo kaakamba wina, 30ni kunamizilana, ni wandhu amuipila Mnungu, ambuli ni kujhidama, ochita voipa ni saavechela obala wao. 31Wopusa, osakhulupilila, alibe lisungu ni akatili. 32Ajhiwa kuti lamulo la Mnungu likamba kuti wandhu akala mtundu umeneo, ifunika afe. Nambho osati vindhu vimenevo achita anyiiwope, nambho avomelezana ni wandhu achita vimeneyo.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Alom 1: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Alom 1
1
1Ine Poolo, Mtumiki wa Yesu Kilisito ni mtumwi nasanghidwa ni kutanidwa ndande ya uthenga wa bwino wa Mnungu.
2Kalepo Mnungu wadaakambila wandhu kuti siwapache Uthenga uwu wabwino, kwa njila ya alosi wake mmalembo ya Mnungu. 3Nghani iyi yabwino imuusu mwana wa Mnungu Yesu kilisito, Mbuye wathu uyo wadabadwa ngati umo wandhu abadwila wadali wa khamu la Daudi, 4ni uyo kwa mbhavu za mzimu woyela, wadamjhiwicha kuti iye ni Mwana wa Mnungu ni kwa kuhyuka kwake, yani Yesu kilisito Mbuye wathu. 5Kwakupitila Yesu Kilisito, ine napachidwa ubwino wokhala mtumiki, ni kwandande yaiye nichogoze wandhu amayiko yonjhe kuti akhoze kukhulupilila ni kuvela Uthenga wa Bwino. 6Anyiimwe Aloma namwe ni amojhi mwa wandhu anyiyawo, mwatanidwa kuti mkhale wandhu wake kilisito mwene.
7Chipano, nikulembelani anyiimwe mwaonjhe muli Ku Loma, anyiimwe Mnungu wakukondani kupunda ni wadakusanghani mkhale wandhu wake mwene,
Nikupembhelani kwa Amnungu Tate wathu mkhale ni ubwino ni mtendele,
Kwaayamika Amnungu
8Poyamba, nimyamika Mnungu wanga kupitila Yesu kilisito ndande yanu mwaonjhe, pakuti kukhulupilila kwanu kuveka pa jhiko lonjhe. 9Mnungu uyo nimtumikila kwa mtima wanga wonjhe, pakuuzila uthenga wa mwana wake, nimmboni wanga kwa umo nikukumbukilani masiku yonjhe mmapembhelo yanga. 10Nimpembha Mnungu wakakonda wanipache malo ya bwino ya kujha kwaanyiimwe chipano. 11Pakuti nikhumbila kupunda kukuonani, kuti nikhoze kukutangatilani kupata mbhaso ya mzimu Woyela ya kukulimbichani chikhulupi chanu. 12Ndiipo anyiimwe pamojhi ni ine, titilane mtima kuti chikhulupi chatu chiime bwino.
13Achabale wanga, nifuna mjhiwe kuti nyengo zambili nidafuna kukuendelani, nambho mbaka sazino nachekelezedwa. Kuti nijhe kukutangatilani kwachita wandhu amkhulupilile Kilisito, ngati umo nidachitila kwa wandhu amayiko yina. 14Ine nifunika nilalikile Uthenga wa Bwino kwa wandhu yawo ali a Agiliki ni wandhu anyiawo osati Agiliki, asoma ni yawo sadasome. 15Ndendande nikumbila kupunda kulalikila uthenga wa bwino kwa anyiimwe muli ku mujhi wa Loma.
Mbhavu ya uthenga wa bwino
16Ine siniona njhoni kuuzila uthenga wa Bwino, wene ni mbhavu ya Mnungu, iyo yaombola wandhu wonjhe amkhulupilila Yesu. Kuyambila Ayahudi ni anyiawo osati ayahudi. 17Pakuti uthenga wa bwino walangiza umo Mnungu wafunila tikhale kuti tivomelezeke pachogolo pake, chindhu ichi chichitika kwa kumkhulupilila Yesu Kilisito, palibe china kupitilila chimecho, ngati umo yalembedwa mmalembo, “Mundhu wovomelezeka kwa Mnungu siwakhale kwa kumkhulupilila Mnungu.”
Kulakwa kwa wandhu
18Kuchokela kumwamba, Mnungu waakwiila wandhu wajha amkana ni achita voipa, anyiyawo kwa njila zao zoipa auchekeleza Uthenga wa Bwino kuti siudajhiwika. 19Vindhu vonjhe va Mnugu vili padanga kwa anyiiwo, ndande Mnungu mwene wadaviika padanga kwao. 20Kuyambila yapo Mnungu wadaumba jhiko, kukhoza kwake ni umnungu wake, ingakhale siuoneka kwa maso, wajhiwikana padanga. Wandhu akhoza kwajhiwa, kuchokana ni vindhu ivo waviumba ndande imeneyo palibe mundhu ata mmojhi wakhoza kukamba sitimjhiwa Mnungu. 21Ingakhale ajhiwa kuti kuli Mnungu, nambho sampacha ulemu uwo ufunika, ni samuyamika mmalo mwake maganizo yawo yali yoipa ni njelu zao zilibe kandhu ni zili ni usabwabwa. 22Achitadama kuti ali ni ekima, nambho ni asabwabwa. 23Asiya kumlambila Mnungu wa muyaya, ni pambuyo pake, avilambila viboliboli vili chifani cha mundhu uyo wamwalila, chifani cha zinyama, mbalami ni vokwawa.
24Ndande imeneyo, Mnungu wasiya achate khumbilo loipa la mitima yao, ni kuchitilana vindhu va njhoni achinawene kwa achinawene. 25Aung'anamula uzene wa Mnungu ni kuuchita ukhale unami, achilemekeza ni kuchilambila choumbidwa ni Mnungu pambuyo pa kumlambila Mnungu mwene, uyo idafukika kulambilildwa muyaya! Ikhale chimwecho.
26Chipano, Mnungu waasiya achate khumbilo loipa. Wachikazi ang'anamula matupi yawo, ni kutumila mosafunikile kwa kukhumbilana achinawene kwa achina wene. 27Ni wachimuna chimwecho, asiya kukhumbilana wamnuna ni wamkazi, akhumbilana anyiiwo kwa anyiiwo. Wachimuna achitilana vindhu va njhoni, chimwecho saalangidwe kuchokana ni vichito vao voipa.
28Pakuti wandhu adakana kumjhiwa Mnungu, Mnungu wasiya mumaganizo yao yoipa, achite vijha siadafunike kuvichita. 29Ajhala kila mtundu wa voipa, chigololo, kuipa, khumbilo loipa, maganizo yoipa. Ajhala njhanjhe, kupha ni ndewo, kunyenga ni ludyo la kukhala ni chuma, ni anyiiwo kaakamba wina, 30ni kunamizilana, ni wandhu amuipila Mnungu, ambuli ni kujhidama, ochita voipa ni saavechela obala wao. 31Wopusa, osakhulupilila, alibe lisungu ni akatili. 32Ajhiwa kuti lamulo la Mnungu likamba kuti wandhu akala mtundu umeneo, ifunika afe. Nambho osati vindhu vimenevo achita anyiiwope, nambho avomelezana ni wandhu achita vimeneyo.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
:
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.