Vichito 20
20
Poolo wayendelanjho mijhi ya Makidoniya ni Ugiliki
1Mkangano wa ku Efeso yapo udatha, Poolo wadaapembha wokhulupila kukomana pamojhi ni iye kuti waalimbikiche ni kulailana nawo. Wadachoka ni kupita kumujhi wa Makidoniya ni ku Giliki. 2Yapo wamapita malo yameneyo, wadaathila mtima kwa mawu yambili anyiwajha adamkhulupilila Yesu. Ndiipo wadafika ku Giliki, 3uko wadakhala miezi itatu. Yapo wamakonjeka kupita ku Silia kwa njila ya sitima, wadazindikila kuti kuli Ayahudi adakhala ni kumpangia mpango woipa. Chimwecho wadalamula kubwelela kwa kupitila ku Makidoniya. 4Poolo wadali pamojhi ni Sopatulo mwana wa Pilo uyo wadachokela ku Beloya, Alisitako ni Sekundo uyo wadachokela ku Tesalonike ni Gayo, mundhu wa ku Delibe, Timoseo pamojhi ni Tikiko ni Tulofino kuchokela malo ya ku Asiya. 5Anyiiwo adachogola ni kutilindilila ife kujha ku Toloa. 6Yapo yadapita masiku yajha ya phwando la mabumunda yopande amila, ife tidakwela sitima kuchokela ku Filipi, niyapo yadata masiku ya sano tidafika ku Oloa. Kumeneko tidakhala jhuma ya mbhumbhu
Poolo wamuhyukicha Elitiko
7Siku limojhinla jhuma, tidakomana pamojhi kuti tidye chakudya. Poolo wamauzila wandhu ni kuyendekela kukamba nawo mbaka usiku pakati, pakuti wadafuna kuchoka siku lochatila. 8Taonjhe tidali ku chumba cha pamwamba pa golofa, ni nyali zambili zimakwelela. 9Chumba cha gholofa, kudali mnyamata mmojhi jhina lake Elitiko. Wadakhala pa dilisha yapo Poolo wamayendekela kwauzila wandhu. Iye wadayamba kuojhela, wadagwa kuchokela ku golofa yakatatu mbaka panjhi. Wandhu yapo adapita kumunyamula, adamkomana wathomwalila. 10Nambho Poolo wadachika panjhi, wadakwatama ni kumkhumbatila mnynamata mmeneyo, niwakamba, “Msadalila, pakuti wakali wamoyo.” 11Ndiipo Poolo wadakwelanjho ku gholofa, wadadya chakudya. Wadayendekela kukamba nawo mbaka malenga kucha, alafu Poolo wadalamula kuchoka. 12Wandhu wajha adamtenga ni kumpekela yujha mnyamata kukhomo wali wamoyo, ni anyiiwo adakondwa kupunda.
Ulendo wa Poolo kuchokela ku Toloa kupita ku Mileto
13Ife tidakwela sitima ni kuchogolela kupita ku Aso uko tidakamtenga Poolo, wadatikambila tichite chimecho pakuti iye wamapita kumeneko pa mwendo. 14Basi wadatipheza kumeneko ku Aso, Poolo wadakwela sitima pamojhi ni ife, ni kupita ku Mitulene. 15Tidachoka kumeneko ni kupita kumalo uko kutanidwa ku Kio. Siku lochatila tidayomboka kupita ku Samo, ni umawa wake tidafika ku mujhi wa Mileto. 16Ndande Poolo wadafuna kuendekela ni ulendo wake, ni siwadafune kupatukila ku Efeso dala siwadachedwa kufika ku Asiya. Iye wamayangu dala wafike chisanga ku Yelusalemu ndande ya pwando la Pentekosite ngati idakakhozeka.
Poolo wakamba ni azee aku Efeso
17Poolo yapo wadali ku Mileto, wadatuma uthenga kupita ku Efeso, kwaatana azee awandhu yawo adamkhulupilila Kilisito kuti akomane naye. 18Yapo adafika wadaakambila, “Anyiimwe mujhiwa umo nidakhala ndhawi yonjhe pakati panu kuyambila siku loyamba yapo nidafika muno mu Asiya. 19Nimjhiwa umo nidamtumikila Mnungu kwa kujhichicha, kwa misozi ni mavuto yayo yadanikomana kuchokana ni mipango ni vindhu voipa ivo adanichitila Ayahudi. 20Mujhiwa kuti sinidakasiya kukulalikilani chindhu chilichonjhe icho chidali chofunikila kwa anyiimwe, nambho nidayaluza padanga ni nyumba kwa nyumba. 21Nidamkambila wandhu wonjhe, Ayahudi ni osati Ayahudi, kuti alape ni amng'anamukile Mnungu, ni mwakhulupilile Ambuye wathu Yesu. 22Nanenjho chipano, nifunika kumvela Mzimu Woyela ni kupita ku Yelusalemu, sinijhiwa icho sichinipate kumeneko. 23Nambho icho nijhiwa ni kuti Mzimu Woyela wanijhiwicha kuti kumangidwa ni mavuto yatonilindilila. 24Nambho ata ngati wandhu sianiphe ine, palibe phindu kwa ine. Nambho icho nichifuna ni kukwanilichape njhito iyo anituma Ambuye Yesu
25“Chipano vechelani, nijhiwa kuti palibe mundhu pakati panu uyo siwanionenjho. Yapo nidali pakati panu nidakulalikilani nghani za Ufumu wa Mnungu. 26Chimwecho nikukambilani lelolino kuti nilibe mlandu kwa mundhu waliyonjhe uyo siwataike pakati panu, 27pakuti nakukambilani vonjhe ivo Mnungu wafuna mchite. 28Chipano, jhipenyeleleni anyiimwe pamojhi ni wandhu wonjhe yawo mwapachidwa ni Mzimu Woyela. Asungeni wandhu amkhulupilila Yesu yawo Amnungu waagula kwa mwazi wa mwana wao. 29Nijhiwa kuti yapo sinichoke kumbuyo kuno siajhe oyaluza amthila yawo ali ngati nghandwe zong'ang'ala pakati panu siajhe ni sakhala ni lisungu ni gulu limenelo. 30Ata pakati pa gulu lanu siachokele wandhu wina yawo siwaayaluze wandhu yawo amkhulupilila Yesu mayaluzo yamthila. Sianyenge wokhulupilila kuti waachate anyiiwo. 31Chimwecho jhipenyeleleni! Mkumbukile kuti sinidasiye kukukumbuchani usiku ni usana kila mmojhi wanu kwa vyaka vitatu ni myezi sita umo wafunikila kukhala.”
32“Chipano nikuikani anyiimwe mu ulonda wa Mnungu ni kwa mawu la chikondi chake, ilo likhoza kukulimbichani ni kukupachani chindhu chijha Mnungu wakamba kuti siwaapache wandhu wake. 33Yapo nidali pamojhi ni anyiimwe, sinidafune myala ya mtengo waukulu kapina madini ya mundhu waliyonjhe kapina njhalu yabwino. 34Mwaachinawene mujhiwa kuti nidachita njhito kwa manja yanga kujhipatila vijha nimavifuna, ni ivo anjhanga amavifuna. 35Siku zonjhe nachita njhito ngati chifani kwanu, kulangiza kuti tifunika kwatangatila osauka, uku nitikumbukila mawu ya Ambuye Yesu mwene yayo yakamba, ‘Ali ni mwawi anyiawo achocha kusiyana ni anyiiawo alandila.’”
36Poolo yapo wadamaliza kukamba chimwechi wadagwada pamojhi ni anyiiwo wonjhe, ndiipo adampembha Mnungu. 37Wandhu wonjhe adalila ni kumvumbatila Poolo, ndiipo adamlaila. 38Icho chidaadandaulicha ni yajha mawu wadaakambila Poolo kuti samuonanjho. Ndiipo adampelekeza mbaka ku sitima.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 20: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.