Vichito 18
18
Poolo waendela mujhi wa Kolinto
1Pambuyo pa yameneyo, Poolo wadachoka ku mujhi wa Asene ni kupita kumujhi wa Kolinto. 2Yapo wadali ku mujhi wa Kolinto wadakomana ni Muyahudi uyo wamatanidwa Akila, uyo wadabadwila mu mujhi wa Ponto, uyo wadali wangofika posachedwa kuchokela ku Italiya pamojhi ni mkazake, pakuti mchogoleli Kilaudia wadalamula Ayahudi onjhe achoke ku Loma. Poolo wadapita kwaayendela anyiiwo, 3Poolo wadakhala kumweko ni kuchita njhito pamojhi ni anyiiwo, pakuti nayo wadali wokonja mahema ngati anyiiwo. 4Poolo wadakamba nawo wandhu mu nyumba yokomanilana Ayahudi kila siku zo Pumulila, kuyesa kwadyelekezela Ayahudi ni agiliki kuti amkhulupilile Yesu.
5Yapo Sila ni Timoseo yapo adafika kuchokela ku Makidoniya, Poolo wadajhichocha kwaalalikila Ayahudi Uthenga wa Mnungu, niwafotokozela kuti Yesu nde Kilisito. 6Ayahudi siadavomelezane ni Poolo ni adayamba kumtukwana. Chimwecho Poolo wadakung'undha lifumbi la njhalu zake kulangiza kuti waakana, niwakambila, “Ngati simuomboledwa, siikhale dala lanu mwaachinawe! Nachita yonjhe yayo nikhoza kuchita. Kuyambila chipano, naapitila wandhu osati Ayahudi.” 7Chimwecho Poolo wadaasiya pamenepo ni kupita kukhala kwa mundhu osati Myahudi, uyo wamatanidwa Tito Yusito, uyo nyumba yake idali pafupi ni ijha nyumba yokomanilana Ayahudi. 8Kilisipo wamkulu wa nyumba yokomanilana Ayahudi, wadaakhulupilila Ambuye iye pamojhi ni wandhu wonjhe amnyumba mwake. Wandhu ambili mmujhi wa Kolinto adavela Uthenga wa Poolo, adamkhulupilila Yesu ni kubatizidwa.
9Siku lomojhi usiku, Ambuye adamkambila Poolo kumaloso, niwakamba, “Usadaopa iwe endekela kwaalikila wandhu siudasiya. 10Ine nili pamojhi ni iwe, ni palibe uyo siwakupweteke iwe. Muli wandhu wanga ambili mmujhi muno.” 11Chimwecho Poolo wadakhala kumeneko kwa chaka chimojhi ni myezi sita niwaayaluza wandhu Uthenga wa Mnungu.
12Galio yapo wadali mlamuli wa jhiko la Akaya, Ayahudi adagwilizana kumgwila Poolo, ni kumpeleka kubwalo la milandu, 13adampacha mlandu kwa kukamba, “Mundhu uyu waanyenga wandhu amlambile Mnungu popande kuchata Thauko la Musa!”
14Poolo yapo wadali siwadakambe chalichonjhe, Galio wadaakambila Ayahudi, “Nidakakuvechelani ngati madandaulo yanu yadakakhala ya volakwa vavikulu kapina wachita chindhu chalichonjhe choipa. 15Nambho chimchijha ngati mchuchanila nghani za majhina ni mau pe, ni kuchuchana kwa mathauko yanu, lamulani mwachinawene wake. Sinifuna kukhala mlamuli wa nghani imeneyo!” 16Ndiipo Wadaatulucha wandhu wajha kubwalo kwa nyumba ya milandu. 17Ndiipo wonjhe kwa pamojhi adamgwila Sositene, wamkulu wa nyumba yokomanilana Ayahudi, adambula pachogolo pa bwalo la milandu, nambho Galio siwadajali kalikonjhe.
Poolo wabwelela ku mujhi wa Antiokiya ya jhiko la Siliya
18Poolo wadakhala ku Kolinto pamojhi ni wandhu adamkhulupila Yesu kwa masiku yambili. Ndiipo wadaalaila wajha wandhu adamkhulupilila Yesu ni kuyamba ulendo panyanja ni kupita ku Siliya, wadachatana ni Pulisila ni Akila. Yapo wadafika ku Kenkelea Poolo wadameta machichi yake kulangiza kuti wakwanilicha chilanga chake kwa Mnungu. 19Ndiipo adafika ku mujhi Efeso, uko Poolo wadaasiya Pulisila ni Akila, nambho iye mwenewake wadalowa mu nyumba yokomanilana Ayahudi ni kukambana nawo. 20Wandhu adampembha Poolo kuti wakhale nawo kwa ndhawi yaitali, nambho wadakana. 21Nambho wadaasiya ni kukamba, “Sinijhenjho kwanu ngati Mnungu siwafune kuti nijhe.” Chimwecho wadakwela Sitima ni kuchoka kujha ku Efeso.
22Yapo wadafika ku Kaisaliya, wadapita ku Yelusalemu kwaalonjela wandhu yawo adamkhulupilia Kilisito, ndiipo wadapita ku Antiokiya. 23Poolo wadakhala ku mujhi wa Antiokiya kwa ndhawi yochepa, ndiipo wadachoka ni kupita jhiko la Galatiya ni Filigiya. Wadayenda ulendo kuchoka mujhi umojhi mbaka mujhi unjake kujha ku Galatiya ni Filigiya. Wamathila mtima wandhu yawo amamkhulupila Kilisito.
Apolo walalikila wandhu ku Efeso ni ku Kolinto
24Ndhawi imeneyo Muyahudi mmojhi uyo watanidwa Apolo, uyo wadabadwila ku Alekezandaliya, wadafika ku mujhi wa Efeso. Mundhu mmeneyo wamajhiwa kukamba bwino, ni wamayajhiwa Malembo ya Mnungu. 25Wadayaluzidwa mayaluzo ya Ambuye, ni ndhawi zonjhe wadakondwela kwaakambila wandhu ghani za Yesu. Icho wadachiyaluza chidali cha uzene, nambho ubatizi uwo wadaujhiwa ingakhale wadaujhiwa ubatizi Yohanape. 26Iye wadayamba kukamba popande mandha mnyumba zokamanilana Ayahudi. Pulisila ni Akila yapo adamvela iye niwakamba, adamtenga kupita nayo kukhomo ni kumfotokozela bwino Malembo ya Mnungu yayo siwamayajhiwe. 27Ndiipo Apolo wadalamula kupita ku Akaya, wokhulupilila aku Efeso adamthila mtima ni kumpacha kalata ya kumjhiwicha kwa achaabale akumeneko kuti amlandile. Yapo wadafika kujha, wadali mthandizo waukulu kupunda kwa wajha adamkhulupilila Yesu ndande ya chikondi cha Ambuye. 28Wadaakhoza ndande wamajhiwa kukamba. Wadachimikiza padanga kuti Ayahudi amalakwicha, adatumila Malembo kulangiza kuti Yesu nde Kilisito.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 18: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Vichito 18
18
Poolo waendela mujhi wa Kolinto
1Pambuyo pa yameneyo, Poolo wadachoka ku mujhi wa Asene ni kupita kumujhi wa Kolinto. 2Yapo wadali ku mujhi wa Kolinto wadakomana ni Muyahudi uyo wamatanidwa Akila, uyo wadabadwila mu mujhi wa Ponto, uyo wadali wangofika posachedwa kuchokela ku Italiya pamojhi ni mkazake, pakuti mchogoleli Kilaudia wadalamula Ayahudi onjhe achoke ku Loma. Poolo wadapita kwaayendela anyiiwo, 3Poolo wadakhala kumweko ni kuchita njhito pamojhi ni anyiiwo, pakuti nayo wadali wokonja mahema ngati anyiiwo. 4Poolo wadakamba nawo wandhu mu nyumba yokomanilana Ayahudi kila siku zo Pumulila, kuyesa kwadyelekezela Ayahudi ni agiliki kuti amkhulupilile Yesu.
5Yapo Sila ni Timoseo yapo adafika kuchokela ku Makidoniya, Poolo wadajhichocha kwaalalikila Ayahudi Uthenga wa Mnungu, niwafotokozela kuti Yesu nde Kilisito. 6Ayahudi siadavomelezane ni Poolo ni adayamba kumtukwana. Chimwecho Poolo wadakung'undha lifumbi la njhalu zake kulangiza kuti waakana, niwakambila, “Ngati simuomboledwa, siikhale dala lanu mwaachinawe! Nachita yonjhe yayo nikhoza kuchita. Kuyambila chipano, naapitila wandhu osati Ayahudi.” 7Chimwecho Poolo wadaasiya pamenepo ni kupita kukhala kwa mundhu osati Myahudi, uyo wamatanidwa Tito Yusito, uyo nyumba yake idali pafupi ni ijha nyumba yokomanilana Ayahudi. 8Kilisipo wamkulu wa nyumba yokomanilana Ayahudi, wadaakhulupilila Ambuye iye pamojhi ni wandhu wonjhe amnyumba mwake. Wandhu ambili mmujhi wa Kolinto adavela Uthenga wa Poolo, adamkhulupilila Yesu ni kubatizidwa.
9Siku lomojhi usiku, Ambuye adamkambila Poolo kumaloso, niwakamba, “Usadaopa iwe endekela kwaalikila wandhu siudasiya. 10Ine nili pamojhi ni iwe, ni palibe uyo siwakupweteke iwe. Muli wandhu wanga ambili mmujhi muno.” 11Chimwecho Poolo wadakhala kumeneko kwa chaka chimojhi ni myezi sita niwaayaluza wandhu Uthenga wa Mnungu.
12Galio yapo wadali mlamuli wa jhiko la Akaya, Ayahudi adagwilizana kumgwila Poolo, ni kumpeleka kubwalo la milandu, 13adampacha mlandu kwa kukamba, “Mundhu uyu waanyenga wandhu amlambile Mnungu popande kuchata Thauko la Musa!”
14Poolo yapo wadali siwadakambe chalichonjhe, Galio wadaakambila Ayahudi, “Nidakakuvechelani ngati madandaulo yanu yadakakhala ya volakwa vavikulu kapina wachita chindhu chalichonjhe choipa. 15Nambho chimchijha ngati mchuchanila nghani za majhina ni mau pe, ni kuchuchana kwa mathauko yanu, lamulani mwachinawene wake. Sinifuna kukhala mlamuli wa nghani imeneyo!” 16Ndiipo Wadaatulucha wandhu wajha kubwalo kwa nyumba ya milandu. 17Ndiipo wonjhe kwa pamojhi adamgwila Sositene, wamkulu wa nyumba yokomanilana Ayahudi, adambula pachogolo pa bwalo la milandu, nambho Galio siwadajali kalikonjhe.
Poolo wabwelela ku mujhi wa Antiokiya ya jhiko la Siliya
18Poolo wadakhala ku Kolinto pamojhi ni wandhu adamkhulupila Yesu kwa masiku yambili. Ndiipo wadaalaila wajha wandhu adamkhulupilila Yesu ni kuyamba ulendo panyanja ni kupita ku Siliya, wadachatana ni Pulisila ni Akila. Yapo wadafika ku Kenkelea Poolo wadameta machichi yake kulangiza kuti wakwanilicha chilanga chake kwa Mnungu. 19Ndiipo adafika ku mujhi Efeso, uko Poolo wadaasiya Pulisila ni Akila, nambho iye mwenewake wadalowa mu nyumba yokomanilana Ayahudi ni kukambana nawo. 20Wandhu adampembha Poolo kuti wakhale nawo kwa ndhawi yaitali, nambho wadakana. 21Nambho wadaasiya ni kukamba, “Sinijhenjho kwanu ngati Mnungu siwafune kuti nijhe.” Chimwecho wadakwela Sitima ni kuchoka kujha ku Efeso.
22Yapo wadafika ku Kaisaliya, wadapita ku Yelusalemu kwaalonjela wandhu yawo adamkhulupilia Kilisito, ndiipo wadapita ku Antiokiya. 23Poolo wadakhala ku mujhi wa Antiokiya kwa ndhawi yochepa, ndiipo wadachoka ni kupita jhiko la Galatiya ni Filigiya. Wadayenda ulendo kuchoka mujhi umojhi mbaka mujhi unjake kujha ku Galatiya ni Filigiya. Wamathila mtima wandhu yawo amamkhulupila Kilisito.
Apolo walalikila wandhu ku Efeso ni ku Kolinto
24Ndhawi imeneyo Muyahudi mmojhi uyo watanidwa Apolo, uyo wadabadwila ku Alekezandaliya, wadafika ku mujhi wa Efeso. Mundhu mmeneyo wamajhiwa kukamba bwino, ni wamayajhiwa Malembo ya Mnungu. 25Wadayaluzidwa mayaluzo ya Ambuye, ni ndhawi zonjhe wadakondwela kwaakambila wandhu ghani za Yesu. Icho wadachiyaluza chidali cha uzene, nambho ubatizi uwo wadaujhiwa ingakhale wadaujhiwa ubatizi Yohanape. 26Iye wadayamba kukamba popande mandha mnyumba zokamanilana Ayahudi. Pulisila ni Akila yapo adamvela iye niwakamba, adamtenga kupita nayo kukhomo ni kumfotokozela bwino Malembo ya Mnungu yayo siwamayajhiwe. 27Ndiipo Apolo wadalamula kupita ku Akaya, wokhulupilila aku Efeso adamthila mtima ni kumpacha kalata ya kumjhiwicha kwa achaabale akumeneko kuti amlandile. Yapo wadafika kujha, wadali mthandizo waukulu kupunda kwa wajha adamkhulupilila Yesu ndande ya chikondi cha Ambuye. 28Wadaakhoza ndande wamajhiwa kukamba. Wadachimikiza padanga kuti Ayahudi amalakwicha, adatumila Malembo kulangiza kuti Yesu nde Kilisito.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
:
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.