Vichito 12
12
Gulu la wandhu amkhulupilila Kilisito livutichidwa
1Masiku yamweyajha mfumu Helode Agilipa wadaagwila ni kuyamba kwaavuticha wandhu akumojhi yawo adamkhulupilila Yesu. 2Wadampha Yakobo mkuluwake wa Yohana kwa upanga. 3Yapo wadaona yayo wachita yaakondwelecha Ayahudi, wadayendekela ni kumgwila Petulo. Ivi vidachitika ndhawi ya pwando la mabumunda yosathila amila. 4Yapo wadamgwila Petulo wadamuika mndende, panjhi pa magulu yanayi ya alonda anayianayi kuti amlonde. Helode wamafuna kumuika Petulo pachogolo pa wandhu dala amlamule pa pwando la Pasaka likali losafike. 5Chimwecho Petulo wadasungidwa mu ndende, nambho ndhawi imwewo, okhulupilila amampembhela kwa Mnungu popande kuleka.
Petulo watuluchidwa kubwalo kwa ndende
6Usiku ujha likali losafike siku ilo Helode wadakamtulucha Petulo kubwalo, Petulo wadagona pakati pa alonda awili. Wadamangidwa maunyolo yawili, ni kudali alonda andhawi imeneyo nialonda khomo la ndende. 7Mwachizulumukila mtumiki wa kumwamba wa Ambuye wadaima pa malo pajha, ni dangalila lidawala mndende mujha. Mtumiki yujha wadamnyukusa Petulo mndhiti ni kumuucha, niwakamba, “Choka chisangha!” Pamwepo maunyolo yajha yadamasuka ni kugwa panjhi. 8Ndiipo mtumiki wa kumwamba wadakamba, “Manga lamba lako ni uvale malapasi yako.” Petulo wadachita chimwecho. Ndiipo mtumiki yujha wadakamba, “Vala khoti lako unichate.” 9Petulo wadamchata mtumiki wa kumwamba kubwalo kwa ndende, popande kujhiwa kuti icho wamachita mtumiki wa kumwamba chidali cha uzene, wamaganiza kuti yadali masombhenya. 10Adapita ulonda woyamba mbaka khomo lakawili la ndende, ni kufika pa khomo la chichulo ilo lipita ku mujhi. Khomo lidachekuka lene, ni anyiiwo adatuluka. Yapo adapita mkwakwa umojhi, yujha mtumiki wa kumwamba wa Mnungu wadamusiya Petulo mwachizulumukila.
11Ndiipo Petulo wadajhiwa icho chidamchitikila, wadakamba, “Chipano najhiwa kuti ni vazene! Ambuye adamtuma mtumiki wa kumwamba wa Mnungu kujha kunichocha ku mbhavu za Helode Agilipa ni kunichocha mu yajha Ayahudi amalindilila yanichitikile.”
12Yapo wadajhiwa chimwecho, Petulo wadajha ku khomo kwa Maliya, amake a Yohana uyo wamatanidwanjho Maliko, uko wandhu ambili adakomana kuchita mapembhelo. 13Petulo wadagogoda chicheko, ni mbowa uyo wamatanidwa Loda wadapita kumvechela. 14Mwali mmeneyo yapo wadajhiwa kuti mvekelo umeneo udali wa Petulo, wadakondwa kwambili, ni wadabwelela popande kuchakula chicheko, ni kwaakambila wandhu kuti, “Petulo waima pakhomo!” 15Anyiiwo adamkambila mwali yujha, “Iwe wobwabwazika eti!” Yapo wadayendekela kuchimikiza kuti ni Petulo, adakamba, “Lazima siwakhale mtumiki wa kumwamba wa Mnungu uwo wamthangatila iye.”
16Nambho Petulo wadayendekela kugogoda chicheko. Pothela adachekula chicheko, ni yapo adamuona Petulo, adazizwa. 17Wadaalangiza chala kuti akhale chete, ni kuyamba kwaafotokozela umo Ambuye umo adamchochela mndende, niwakamba, “Mwaakambile Yakobo ni wandhu wina yawo adamkhulupilila Kilisito nghani izi.” Ndiipo wadachoka ni kupita kumalo yanjake.
18Umawa yapo udafika asikali wajha adali ni mandha yayakulu ndande ya yayo yachitika kwa Petulo. 19Helode wadaalamula kuti amufunefune Petulo, nambho saadampheze. Ndiipo wadaafunjhichicha anyiwajha alonda ni kulamula kuti aphedwe.
Yapo yadapita yaya, Helode wadachoka ku Yudea ni kupita kukhala ku Kaisaliya kwa ndhawi.
Mfumu Helode Agilipa wamwalila
20Helode wadakwiichidwa kupunda ni wandhu a ku Tilo ni Sidoni. Chimwecho wandhu adapita kukamuona iye mmagulumagulu. Adakambana ni Bulasito, mbowa wamkulu wa Holode uyo wadamkhulupilila, ni wadavomela kwaathangatila. Ndiipo Bulasito wadapita kwa Helode ni kupembha mtendele, pakuti jhiko lawo limapata chakudya kuchokela ku jhiko la mfumu Helode.
21Basi yapo lidafika siku ilo adagwilizana kukomana, mfumu Helode Agilipa wadavala njhalu yachifumu ni kukhala pampando wachifumu, ni kuyamba kukamba ni wandhu. 22Wandhu yawo adasonghana pajha adabula phokoso niakamba, “Uwu osati mvekelo wa mundhu, nambho ni mvekelo wa mnungu!” 23Pamwepo mtumiki wa kumwamba wa Ambuye wadamgwecha Helode panjhi ndande siwadamtamande Mnungu. Wadagwilidwa ni utenda wa mwela ni kumwalila.
24Nambho Mawu la Mnungu lidayendekela kuyenela ni kukula.
25Banaba ni Saulo yapo adamaliza njhito ya Mnungu, adachoka ku Yelusalemu ali pamojhi ni Yohana uyo wamatanidwa Maliko.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
Vichito 12: NTNYBL2025
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Vichito 12
12
Gulu la wandhu amkhulupilila Kilisito livutichidwa
1Masiku yamweyajha mfumu Helode Agilipa wadaagwila ni kuyamba kwaavuticha wandhu akumojhi yawo adamkhulupilila Yesu. 2Wadampha Yakobo mkuluwake wa Yohana kwa upanga. 3Yapo wadaona yayo wachita yaakondwelecha Ayahudi, wadayendekela ni kumgwila Petulo. Ivi vidachitika ndhawi ya pwando la mabumunda yosathila amila. 4Yapo wadamgwila Petulo wadamuika mndende, panjhi pa magulu yanayi ya alonda anayianayi kuti amlonde. Helode wamafuna kumuika Petulo pachogolo pa wandhu dala amlamule pa pwando la Pasaka likali losafike. 5Chimwecho Petulo wadasungidwa mu ndende, nambho ndhawi imwewo, okhulupilila amampembhela kwa Mnungu popande kuleka.
Petulo watuluchidwa kubwalo kwa ndende
6Usiku ujha likali losafike siku ilo Helode wadakamtulucha Petulo kubwalo, Petulo wadagona pakati pa alonda awili. Wadamangidwa maunyolo yawili, ni kudali alonda andhawi imeneyo nialonda khomo la ndende. 7Mwachizulumukila mtumiki wa kumwamba wa Ambuye wadaima pa malo pajha, ni dangalila lidawala mndende mujha. Mtumiki yujha wadamnyukusa Petulo mndhiti ni kumuucha, niwakamba, “Choka chisangha!” Pamwepo maunyolo yajha yadamasuka ni kugwa panjhi. 8Ndiipo mtumiki wa kumwamba wadakamba, “Manga lamba lako ni uvale malapasi yako.” Petulo wadachita chimwecho. Ndiipo mtumiki yujha wadakamba, “Vala khoti lako unichate.” 9Petulo wadamchata mtumiki wa kumwamba kubwalo kwa ndende, popande kujhiwa kuti icho wamachita mtumiki wa kumwamba chidali cha uzene, wamaganiza kuti yadali masombhenya. 10Adapita ulonda woyamba mbaka khomo lakawili la ndende, ni kufika pa khomo la chichulo ilo lipita ku mujhi. Khomo lidachekuka lene, ni anyiiwo adatuluka. Yapo adapita mkwakwa umojhi, yujha mtumiki wa kumwamba wa Mnungu wadamusiya Petulo mwachizulumukila.
11Ndiipo Petulo wadajhiwa icho chidamchitikila, wadakamba, “Chipano najhiwa kuti ni vazene! Ambuye adamtuma mtumiki wa kumwamba wa Mnungu kujha kunichocha ku mbhavu za Helode Agilipa ni kunichocha mu yajha Ayahudi amalindilila yanichitikile.”
12Yapo wadajhiwa chimwecho, Petulo wadajha ku khomo kwa Maliya, amake a Yohana uyo wamatanidwanjho Maliko, uko wandhu ambili adakomana kuchita mapembhelo. 13Petulo wadagogoda chicheko, ni mbowa uyo wamatanidwa Loda wadapita kumvechela. 14Mwali mmeneyo yapo wadajhiwa kuti mvekelo umeneo udali wa Petulo, wadakondwa kwambili, ni wadabwelela popande kuchakula chicheko, ni kwaakambila wandhu kuti, “Petulo waima pakhomo!” 15Anyiiwo adamkambila mwali yujha, “Iwe wobwabwazika eti!” Yapo wadayendekela kuchimikiza kuti ni Petulo, adakamba, “Lazima siwakhale mtumiki wa kumwamba wa Mnungu uwo wamthangatila iye.”
16Nambho Petulo wadayendekela kugogoda chicheko. Pothela adachekula chicheko, ni yapo adamuona Petulo, adazizwa. 17Wadaalangiza chala kuti akhale chete, ni kuyamba kwaafotokozela umo Ambuye umo adamchochela mndende, niwakamba, “Mwaakambile Yakobo ni wandhu wina yawo adamkhulupilila Kilisito nghani izi.” Ndiipo wadachoka ni kupita kumalo yanjake.
18Umawa yapo udafika asikali wajha adali ni mandha yayakulu ndande ya yayo yachitika kwa Petulo. 19Helode wadaalamula kuti amufunefune Petulo, nambho saadampheze. Ndiipo wadaafunjhichicha anyiwajha alonda ni kulamula kuti aphedwe.
Yapo yadapita yaya, Helode wadachoka ku Yudea ni kupita kukhala ku Kaisaliya kwa ndhawi.
Mfumu Helode Agilipa wamwalila
20Helode wadakwiichidwa kupunda ni wandhu a ku Tilo ni Sidoni. Chimwecho wandhu adapita kukamuona iye mmagulumagulu. Adakambana ni Bulasito, mbowa wamkulu wa Holode uyo wadamkhulupilila, ni wadavomela kwaathangatila. Ndiipo Bulasito wadapita kwa Helode ni kupembha mtendele, pakuti jhiko lawo limapata chakudya kuchokela ku jhiko la mfumu Helode.
21Basi yapo lidafika siku ilo adagwilizana kukomana, mfumu Helode Agilipa wadavala njhalu yachifumu ni kukhala pampando wachifumu, ni kuyamba kukamba ni wandhu. 22Wandhu yawo adasonghana pajha adabula phokoso niakamba, “Uwu osati mvekelo wa mundhu, nambho ni mvekelo wa mnungu!” 23Pamwepo mtumiki wa kumwamba wa Ambuye wadamgwecha Helode panjhi ndande siwadamtamande Mnungu. Wadagwilidwa ni utenda wa mwela ni kumwalila.
24Nambho Mawu la Mnungu lidayendekela kuyenela ni kukula.
25Banaba ni Saulo yapo adamaliza njhito ya Mnungu, adachoka ku Yelusalemu ali pamojhi ni Yohana uyo wamatanidwa Maliko.
ទើបបានជ្រើសរើសហើយ៖
:
គំនូសចំណាំ
ចែករំលែក
ចម្លង
ចង់ឱ្យគំនូសពណ៌ដែលបានរក្សាទុករបស់អ្នក មាននៅលើគ្រប់ឧបករណ៍ទាំងអស់មែនទេ? ចុះឈ្មោះប្រើ ឬចុះឈ្មោះចូល
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.