1
Mk. 14:36
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Adanenanso kuti, “Abba, Atate, mungathe kuchita chilichonse. Mundichotsere chikho cha masautsochi. Komabe chitani zimene mukufuna Inu, osati zimene ndikufuna Ine ai.”
مقایسه
Mk. 14:36 را جستجو کنید
2
Mk. 14:38
Khalani maso inu ndi kumapemphera, kuti mungagwe m'zokuyesani. Mtima ndiye ukufunitsitsadi, koma langokhala lofooka ndi thupi.”
Mk. 14:38 را جستجو کنید
3
Mk. 14:9
Ndithu ndikunenetsa kuti kulikonse kumene anthu azikalalika Uthenga Wabwino pa dziko lonse lapansi, azidzafotokozanso zimene maiyu wachita, kuti anthu azidzamkumbukira.”
Mk. 14:9 را جستجو کنید
4
Mk. 14:34
Adaŵauza kuti, “Mumtima mwanga muli chisoni chachikulu chofa nacho. Inu khalani pompano, koma mukhale masotu.”
Mk. 14:34 را جستجو کنید
5
Mk. 14:22
Iwo alikudya choncho, Yesu adatenga mkate, nathokoza Mulungu, nkuunyemanyema, nagaŵira ophunzira aja, ndipo adati, “Kwayani, ili ndi thupi langa.”
Mk. 14:22 را جستجو کنید
6
Mk. 14:23-24
Kenaka adatenga chikho, nathokoza Mulungu, nkuchipereka kwa ophunzirawo, naamwa onse. Ndipo adaŵauza kuti, “Aŵa ndi magazi anga otsimikiza Chipangano cha Mulungu. Magazi ameneŵa ndiŵakhetsa chifukwa cha anthu ochuluka.
Mk. 14:23-24 را جستجو کنید
7
Mk. 14:27
Pambuyo pake Yesu adauza ophunzira ake kuti, “Nonsenu mukhumudwa nane nkundisiya. Paja Malembo akuti, ‘Ndidzapha mbusa, ndipo nkhosa zidzangoti balala.’
Mk. 14:27 را جستجو کنید
8
Mk. 14:42
Dzukani, tiyeni tizipita. Suuyu wodzandipereka uja, wafika.”
Mk. 14:42 را جستجو کنید
9
Mk. 14:30
Yesu adamuuza kuti, “Ndithu ndikunenetsa kuti lero lomwe lino usiku womwe uno, tambala asanalire kachiŵiri, ukhala utandikana katatu kuti Ine sundidziŵa.”
Mk. 14:30 را جستجو کنید