1
Miyambo 22:6
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Compare
Explore Miyambo 22:6
2
Miyambo 22:4
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Explore Miyambo 22:4
3
Miyambo 22:1
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Explore Miyambo 22:1
4
Miyambo 22:24
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Explore Miyambo 22:24
5
Miyambo 22:9
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Explore Miyambo 22:9
6
Miyambo 22:3
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Explore Miyambo 22:3
7
Miyambo 22:7
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Explore Miyambo 22:7
8
Miyambo 22:2
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Explore Miyambo 22:2
9
Miyambo 22:22-23
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu, pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
Explore Miyambo 22:22-23