Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka,
chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu.
Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye,
ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye.
Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona,
ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.