1
Zek. 9:9
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Kondwani kwambiri, inu anthu a ku Ziyoni. Fuulani kwambiri, inu anthu a ku Yerusalemu. Onani, mfumu yanu ikudza kwa inu. Ikubwera ili yopambana ndi yogonjetsa adani. Ndi yodzichepetsa ndipo yakwera pa bulu, bulu wake kamwana tsono.
مقایسه
Zek. 9:9 را جستجو کنید
2
Zek. 9:10
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efuremu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu. Uta wankhondo adzauthyola. Mfumu yanu idzachititsa mtendere pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndiponso kuchokera ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku mathero a dziko lapansi.
Zek. 9:10 را جستجو کنید
3
Zek. 9:16
Tsiku limenelo Chauta, Mulungu wao, adzaŵapulumutsa, pakuti anthu akewo ali ngati nkhosa. M'dziko laolo anthuwo adzakhala onyezimira ngati miyala ya mtengo wapatali ya pa chisoti chaufumu.
Zek. 9:16 را جستجو کنید