1
Mk. 8:35
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Chifukwa wofuna kupulumutsa moyo wake, adzautaya, koma wotaya moyo wake chifukwa cha Ine ndi Uthenga Wabwino, adzaupulumutsa.
مقایسه
Mk. 8:35 را جستجو کنید
2
Mk. 8:36
Nanga ndiye kuti munthu wapindulanji atapata zonse za pansi pano, iyeyo nkutaya moyo wake?
Mk. 8:36 را جستجو کنید
3
Mk. 8:34
Pambuyo pake Yesu adaitana khamu la anthu pamodzi ndi ophunzira aja kuti adze pafupi naye, ndipo adaŵauza kuti, “Munthu wofuna kutsana Ine, adzikane mwiniwakeyo, ndipo asenze mtanda wake nkumanditsata.
Mk. 8:34 را جستجو کنید
4
Mk. 8:37-38
Munthu angalipire chiyani choti aombolere moyo wake? Tsono ngati munthu achita manyazi ndi Ine ndiponso ndi mau anga pamaso pa anthu ochimwa a makonoŵa amene ali osakhulupirika, ameneyo nanenso Mwana wa Munthune ndidzachita naye manyazi pamene ndidzabwera pamodzi ndi angelo oyera, ndili ndi ulemerero wa Atate anga.”
Mk. 8:37-38 را جستجو کنید
5
Mk. 8:29
Apo Yesu adaŵafunsa kuti, “Nanga inuyo, mumati ndine yani?” Petro adamuyankha kuti, “Inu ndinu Mpulumutsi wolonjezedwa uja.”
Mk. 8:29 را جستجو کنید