YouVersion Logo
Search Icon

Alom 16

16
Moni kwa wandhu osiyana siyana
1Nikonda kumjhiwicha kwanu mlongo wathu Foibe, uyo wali mtumiki pa gulu la wandhu amkhulupilila Yesu ku Kenikelea. 2Nikupembhani mlandileni bwino ndande waakhupilila Ambuye ngati umo ifunikila kwaalandila wandhu a Mnungu, mpacheni chalichonjhe icho siwachifune, pakuti iye wakhala wabwino kupunda kwa wandhu ambili ni kwaine. 3Moni zanga zafikile Pulisila ni Akila, opota njhito anjanga pa utumiki wa Kilisito Yesu. 4Adali tayali ata kumwalila ndande ya ine. Niyamika achameneo ni magulu yonjhe ya wandhu yawo amkhulupilila Yesu mmaiko yina yayamika anyiiwo. 5Walonjele wandhu amkhulupilila Yesu yawo apezana kukhomo kwako.
Moni zanga zimfikile mbwenji wanga Epaineto uyo wadali woyamba ku mkhulupilila Yesu ku jhiko la Asia 6Mnilonjelele Maliya uyo wachita njhito kwa mtima ndande yanu. 7Mumlonjele Anduloniko ni Yunia, Aizilaeli achanjanga yawo adamangidwa mndende pamojhi niine, anyiiwo ajhiwika kupunda pakati pa atumwi, chimchijha adanichogolela ine kumkhulupilila Kilisito.
8Munilonjelele mbwenji wanga Ampiliato, mnjanga pakulunjana ni Kilisito. 9Munilonjelele Ulibano, uyo tipota taonjhe njhito ya kumtumikila kilisito, munilonjelelenjho mbwenji langa Sitaku. 10Munilonjelele Apele uyo walangiza kuti wakhulupilika ni Kilisito. Munilonjelele wonjhe ali akhala mnyumba mwa Alistobulo. 11Munilonjelele mbale wanga Helodiana, ni wandhu wonjhe yawo akhala mnyumba ya Nalikishi yawo akhulupilila Ambuye.
12Munilonjelele Tilufena ni Tilufosa wachikazi anyiwajha achita njhito ya kwatumikila Ambuye kwa mtima, mlonjeleni mbwenji wanga Pelisi wamkazi mwina uyo wadachita njhito kwa mtima ndande ya Ambuye. 13Mnilonjelele Lufo, mundhu wadasanghidwa ni Ambuye, ni maye wake yawo ali maye wanga niine. 14Mnilonjelele ni Asunikilisito, Flegoni, Helome, Patiloba Helima, ni abale wonjhe ali pamojhi ni iwo. 15Mnilonjelele ni Fiologo ni Yulia, Nelea ni mlongo wake ni Olimpa, ni wandhu wonjhe a Mnungu ali pamojhi ni anyiiwo. 16Mlonjelane anyiimwe kwa anyiimwe kwa chizindikilo cha kulangiza kuti mkondana. Nianyiimwe akulonjeleni magulu ya wandhu amkhulupilila Yesu Kilisito kuchokela mmalo yosiyana siyana.
Poolo wamalizila maagizo
17Nikupembhani achabale wanga mkhale maso ni anyiwajha apeleka kupatukana ni kwachita wandhu wina asiye chikhulupililo, ni anyiyawo achucha mayaluzo yayo mdayaluzidwa mkakhale patali nawo. 18Pakuti wandhu amtundu umeneo simtumikila Kilisito Ambuye, nambho ajhikondwelecha achina wene. Kwamawu yao yokoma ni mayaluzo yawo yopembelela achita wandhu Amnungu apanduke. 19Kila mundhu wavela umo mumvechela Ambuye, nambho sinikondwele kwa umo mchitila vindhu vabwino ni popande kulakwa kapina kuchita vindhu voipa. 20Niiye Mnungu uyo wapeleka mtendele siwachedwa kumpondela satana panjhi pa mwendo yanu,
mwawi wa Ambuye wathu Yesu kilisito ikhale ni anyiimwe.
21Chimchijha Timotheo wopota njhito mnjanga wakulonjelani. Lukio, Yasoni ni Sosipateli, abale wanga akulonjelani.
22Niine Telitio, nalemba kalata ino, nikulonjelani kwa jhina la Ambuye.
23Gayo uyo wanilandila, pamojhi ni gulu lonjhe la wandhu yawo amkhulupilila Yesu apezana kwaiye akulonjelani, wakulonjelani Elasito, uyo wasunga ndalama mumujhi uno, wakulonjelani Kwalito mbale wathu. 24Ubwino wa Ambuye watu Yesu Kilisito ukhale pamojhi nianyiimwe. Ikhale chimwecho.
Poolo wamtamanda Mnungu
25Chipano wakwezedwe Mnungu uyo wakhoza kukuchitani anyiimwe mkhale nganganga mchikhulupililo ndande ya ujha Uthenga wa Bwino wa Yesu nidakulalikilani, kuchokana ni kuvunukuludwa visisi vidabisika kuyambila kale. 26Nambho chipano uzene uwu wavunukulidwa kwa njila ya malembo ya alosi, ni kwa lamulo la Mnungu wa muyaya wajhiwichidwa kwa maiko yonjhe, kuti wonjhe akhoze kukhulupilila Yesu Kilisito ni kuchita icho wachifuna.
27Mnungu wali yokha ni uyo wali ni njelu zonjhe watamandidwe kupitila Yesu Kilisito, muyaya ni muyaya! Ikhale chimwecho.

Currently Selected:

Alom 16: NTNYBL2025

Highlight

Share

Copy

None

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in