Matayo 25
25
Chifani cha anamwali khumi
1“Ndhawi imeneyo, ufumu wakumwamba siulingane ni anamwali kumi atenga nyali zao nikupita kumlandila okwata. 2Anamwali asano pakati pao adali asabobwa ni asano adali ni njelu. 3Anamwali asabobwa wajha adatenga nyali zao nambho sadatenga mafuta ina, 4Nambho anyiwaja adali ninjelu adatenga mabotolo yayo yadajhala mafuta ni pamojhi nyali zao. 5Okwata wadachedwa kujha ni anamwali wonjhe adaojhela ni kugona.
6“Usiku pakati padaveka mundhu niwaluluta ndhungululu, ‘lyaa, lyaa! Mwene ukwati uyuyapa, tieni timlandile iye.’ 7Ndiipo anamwali wonjhe adauka ni kuzikonja nyali zao dala zikwelele bwino. 8Anamwali asabobwa wajha adaakambila anamwali anjelu, ‘Tigawileni mafuta yanu pang'ono, nyali zathu zitothima.’ 9Anamwali a njelu wajha adaayangha, ‘Notho, siyatikwana kupungulana ife ni anyiimwe. Mbasa mpite kwa wandhu yawo agulicha mafuta mkagule yanu.’ 10Yapo amapita kugula mafuta, kumbuyo kwao okwata wadafika, anamwali anjelu wajha adajhikonjekela adalowa pamojhi ni okwata kuphwando la ukwati ni chicheko chidachekedwa.”
11“Pambuyo pang'ono, adajha anamwali asabobwa wajha, adatana, ‘Imwe wakulu, imwe wakulu! Tichakulileni chicheko!’ 12Nambho wokwata yujha wadayangha kuti siwajhiwa ata pang'ono.”
13Ndiipo Yesu wadamalizila kukamba, “Mjhipenyelele pakuti simujhiwa siku kapina saa.”
Chifani cha mbowa atatu
Luka 19:11-27
14“Chinchijha, ufumu wa Mnungu ulingana ni mundhu wadapita ku ulendo ni kwaika mbowa wake kuti aimilile chuma chake. 15Wadampacha kila mmojhi kulingana ni umo wakhozela. Mmojhi wadampacha timathumba tisano ta zahabu, mwina timathumba elufu ziwili ta zahabu, ni mwina timathumba elufu imojhi ta zahabu. Ndiipo iye wadachoka kupita ku ulendo. 16Yujha wadalandila tmatumba tisano ta zahabu, wadapita kuchita malonda ni wadabalicha timatumba tina ta tisano ta zahabu. 17Chimchijha mbowa yujha wadalandila matumba yawili, wadayabalicha, yadaongezeka matumba ina yawili ya zahabu. 18Nambho yujha wadalandila kathumba kamojhi ka zahabu, wadachoka ni kupita kukumba jhenje ni kukakwilila kajha kathumba ka zahabu wadapachidwa ni mkulu wake.
19“Yapo yadatha masiku yambili, yujha wamkulu wake wadabwela ni kufuna kujhiwa ghani ya chuma chake. 20Mbowa yujha wadalandila timatumba tisano, wadajha kupeleka timatumba tina tisano ta zahabu, uku ni wadakamba, ‘Iwe mbuye udanipacha timatumba tisano ta zahabu, penyani napeleka timatumba tina tisano ta zahabu.’ 21Mkulu wake wadamkambila, ‘Wachita bwino, iwe ni mbowa wabwino ni ukhulupilika. Pakuti udakhulupilika kwa vindhu vochepa, chipano sinikupache vindhu va vikulu, majha ukondwele pamojhi ni mkulu wako!’ 22Ndiipo wadajha yujha mbowa wadalandila timatumba tiwili ta zahabu, wadakamba, ‘Iwe mbuye udanipacha timatumba tiwili ta zahabu, kaonani napatanjho timathumba tiwili ta zahabu,’ 23Mkulu wake wadakamba, ‘Wachita bwino, iwe ni mbowa wabwino ni okhulupilika. Pakuti udali wokhulupilika kwa vindhu vochepa, sinikuike uimilile vindhu va vikulu, majha ukondwele pamojhi ni mkulu wako!’ 24Ndiipo wadajha yujha mbowa wadalandila kathumba kamojhi ka zahabu, wadakamba, ‘Iwe mbuye, nijhiwa iwe nimundhu wopande lisungu, ukolola yapo siuda vyale ukokola yapo siudamwaze, 25Nidaopa, nidapita kubisa kathumba kanu ka zahabu pandhaka. Ili yapo kathumba kanu ka zahabu.’ 26Mkulu wake wadamyangha, ‘Iwe mbowa woipa ni mlesi! Ujhiwa kuti ine nikolola yapo sinida vyale ni kukusa yapo sinida vyale mbeu? 27Udafunika ukapache kathumba kako ka zahabu wandhu yawo aghulicha zahabu, kuti yapo sinibwele nipate phindu. 28Mlandeni kathumba ka zahabu, ni mumpache yujha wali ni timathumba khumi ta zahabu. 29Pakuti kila uyo wachitila njhito icho nampacha sinimchuluchile vina nayo siwakhale navo vambili. Nambho mundhu waliyonjhe uyo siwachitila njhito icho nimpacha, ata chaching'ono walinacho siwalandidwe. 30Mbowa uyu woipa, mtaeni kubwalo kumdima uko sikukhale chililo ni kubukutula mano.’”
Lamulo lotela la mayiko!
31“Mwana wa Mundhu yapo siwajhe muulemelelo wake pamojhi ni atumiki a kumwamba a Mnungu, onjhe pamojhi naye yapo siwakhale pampando wa ufumu uku wali mfumu. 32Wandhu wonjhe a maiko siyasonghane pamaso pake, ni naye siwapatule ngati owesa mbelele umo wapatula mbelele ni mbuzi. 33Siwaziike mbelele kwene, ni mbuzi kumanjele. 34Ndiipo mfumu siwakambile anyiwajha ali kwene, ‘Majhani anyiimwe mwapachidwa mwawi ni Atate kulandila ufumu waikidwa anyiimwe kuyambila kuumbidwa kwa jhiko. 35Nidali ni njala mdanipacha chakudya, ni nidali nilujho mdanipacha majhi ya kumwa, ni nidali mlendo mdanilandila mnyumba zanu. 36Nidalibe njhalu mdaniveka, nidali odwala mdanidwaza ni nidali mndende mdaniyendela.’ 37Pamenepo wandhu abwino siamuyanghe Mbuye, ‘Liti tidakuonani muli ninjala tidakupachani chakudya ni liti mudali ni lujho tidakupachani majhi ya kumwa? 38Liti tidakuonani mwali alendo niife kukulandilani kapina udalibe njhalu ni tidakupacha njhalu? 39Liti mumadwala kapina mwamangidwa mndende tidakuyendelani?’ 40Mfumu siwaayanghe, ‘Zene nikukambilani, umo mwamchitila mmojhi wa anyiyawa abale wanga yawo sajhikoza, mwanichitila ine!’”
41“Ndiipo siwakambile wajha ali kumanjele, ‘Chokani kwanga anyimwe mwalosedwa, pitani kumoto wa muyaya waikilidwa Satana ni atumiki wake! 42Nidali ni njala anyiimwe simudanipache chakudya, nidali ni lujho anyiimwe simudanipache majhi, 43nidali mlendo anyiimwe simudanilandile, nidalibe njhalu anyiimwe simudanipache, nidali odwala ni nidali mndende anyiimwe simudajhe kuniyendela.’ 44Ndiipo naonjho siamuyanghe, ‘Ambuye, liti tidakuonani imwe muli ni njala kapina muli ni lujho kapina mwali alendo kapina mudalibe njhalu kapina muli odwala ni muli mndende sitidakutangatileni?’ 45Mfumu siwaayanghe, ‘Zene nikukambilani, ngati mudakana kwaathangatila mmojhi wa waang'ono yawa, mwanichitila ine.’ 46Anyiyawa siapelekdwe kuchilango cha muyaya, nambho anyiwajha wandhu abwino siapite ku umoyo wa muyaya.”
Currently Selected:
Matayo 25: NTNYBL2025
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Matayo 25
25
Chifani cha anamwali khumi
1“Ndhawi imeneyo, ufumu wakumwamba siulingane ni anamwali kumi atenga nyali zao nikupita kumlandila okwata. 2Anamwali asano pakati pao adali asabobwa ni asano adali ni njelu. 3Anamwali asabobwa wajha adatenga nyali zao nambho sadatenga mafuta ina, 4Nambho anyiwaja adali ninjelu adatenga mabotolo yayo yadajhala mafuta ni pamojhi nyali zao. 5Okwata wadachedwa kujha ni anamwali wonjhe adaojhela ni kugona.
6“Usiku pakati padaveka mundhu niwaluluta ndhungululu, ‘lyaa, lyaa! Mwene ukwati uyuyapa, tieni timlandile iye.’ 7Ndiipo anamwali wonjhe adauka ni kuzikonja nyali zao dala zikwelele bwino. 8Anamwali asabobwa wajha adaakambila anamwali anjelu, ‘Tigawileni mafuta yanu pang'ono, nyali zathu zitothima.’ 9Anamwali a njelu wajha adaayangha, ‘Notho, siyatikwana kupungulana ife ni anyiimwe. Mbasa mpite kwa wandhu yawo agulicha mafuta mkagule yanu.’ 10Yapo amapita kugula mafuta, kumbuyo kwao okwata wadafika, anamwali anjelu wajha adajhikonjekela adalowa pamojhi ni okwata kuphwando la ukwati ni chicheko chidachekedwa.”
11“Pambuyo pang'ono, adajha anamwali asabobwa wajha, adatana, ‘Imwe wakulu, imwe wakulu! Tichakulileni chicheko!’ 12Nambho wokwata yujha wadayangha kuti siwajhiwa ata pang'ono.”
13Ndiipo Yesu wadamalizila kukamba, “Mjhipenyelele pakuti simujhiwa siku kapina saa.”
Chifani cha mbowa atatu
Luka 19:11-27
14“Chinchijha, ufumu wa Mnungu ulingana ni mundhu wadapita ku ulendo ni kwaika mbowa wake kuti aimilile chuma chake. 15Wadampacha kila mmojhi kulingana ni umo wakhozela. Mmojhi wadampacha timathumba tisano ta zahabu, mwina timathumba elufu ziwili ta zahabu, ni mwina timathumba elufu imojhi ta zahabu. Ndiipo iye wadachoka kupita ku ulendo. 16Yujha wadalandila tmatumba tisano ta zahabu, wadapita kuchita malonda ni wadabalicha timatumba tina ta tisano ta zahabu. 17Chimchijha mbowa yujha wadalandila matumba yawili, wadayabalicha, yadaongezeka matumba ina yawili ya zahabu. 18Nambho yujha wadalandila kathumba kamojhi ka zahabu, wadachoka ni kupita kukumba jhenje ni kukakwilila kajha kathumba ka zahabu wadapachidwa ni mkulu wake.
19“Yapo yadatha masiku yambili, yujha wamkulu wake wadabwela ni kufuna kujhiwa ghani ya chuma chake. 20Mbowa yujha wadalandila timatumba tisano, wadajha kupeleka timatumba tina tisano ta zahabu, uku ni wadakamba, ‘Iwe mbuye udanipacha timatumba tisano ta zahabu, penyani napeleka timatumba tina tisano ta zahabu.’ 21Mkulu wake wadamkambila, ‘Wachita bwino, iwe ni mbowa wabwino ni ukhulupilika. Pakuti udakhulupilika kwa vindhu vochepa, chipano sinikupache vindhu va vikulu, majha ukondwele pamojhi ni mkulu wako!’ 22Ndiipo wadajha yujha mbowa wadalandila timatumba tiwili ta zahabu, wadakamba, ‘Iwe mbuye udanipacha timatumba tiwili ta zahabu, kaonani napatanjho timathumba tiwili ta zahabu,’ 23Mkulu wake wadakamba, ‘Wachita bwino, iwe ni mbowa wabwino ni okhulupilika. Pakuti udali wokhulupilika kwa vindhu vochepa, sinikuike uimilile vindhu va vikulu, majha ukondwele pamojhi ni mkulu wako!’ 24Ndiipo wadajha yujha mbowa wadalandila kathumba kamojhi ka zahabu, wadakamba, ‘Iwe mbuye, nijhiwa iwe nimundhu wopande lisungu, ukolola yapo siuda vyale ukokola yapo siudamwaze, 25Nidaopa, nidapita kubisa kathumba kanu ka zahabu pandhaka. Ili yapo kathumba kanu ka zahabu.’ 26Mkulu wake wadamyangha, ‘Iwe mbowa woipa ni mlesi! Ujhiwa kuti ine nikolola yapo sinida vyale ni kukusa yapo sinida vyale mbeu? 27Udafunika ukapache kathumba kako ka zahabu wandhu yawo aghulicha zahabu, kuti yapo sinibwele nipate phindu. 28Mlandeni kathumba ka zahabu, ni mumpache yujha wali ni timathumba khumi ta zahabu. 29Pakuti kila uyo wachitila njhito icho nampacha sinimchuluchile vina nayo siwakhale navo vambili. Nambho mundhu waliyonjhe uyo siwachitila njhito icho nimpacha, ata chaching'ono walinacho siwalandidwe. 30Mbowa uyu woipa, mtaeni kubwalo kumdima uko sikukhale chililo ni kubukutula mano.’”
Lamulo lotela la mayiko!
31“Mwana wa Mundhu yapo siwajhe muulemelelo wake pamojhi ni atumiki a kumwamba a Mnungu, onjhe pamojhi naye yapo siwakhale pampando wa ufumu uku wali mfumu. 32Wandhu wonjhe a maiko siyasonghane pamaso pake, ni naye siwapatule ngati owesa mbelele umo wapatula mbelele ni mbuzi. 33Siwaziike mbelele kwene, ni mbuzi kumanjele. 34Ndiipo mfumu siwakambile anyiwajha ali kwene, ‘Majhani anyiimwe mwapachidwa mwawi ni Atate kulandila ufumu waikidwa anyiimwe kuyambila kuumbidwa kwa jhiko. 35Nidali ni njala mdanipacha chakudya, ni nidali nilujho mdanipacha majhi ya kumwa, ni nidali mlendo mdanilandila mnyumba zanu. 36Nidalibe njhalu mdaniveka, nidali odwala mdanidwaza ni nidali mndende mdaniyendela.’ 37Pamenepo wandhu abwino siamuyanghe Mbuye, ‘Liti tidakuonani muli ninjala tidakupachani chakudya ni liti mudali ni lujho tidakupachani majhi ya kumwa? 38Liti tidakuonani mwali alendo niife kukulandilani kapina udalibe njhalu ni tidakupacha njhalu? 39Liti mumadwala kapina mwamangidwa mndende tidakuyendelani?’ 40Mfumu siwaayanghe, ‘Zene nikukambilani, umo mwamchitila mmojhi wa anyiyawa abale wanga yawo sajhikoza, mwanichitila ine!’”
41“Ndiipo siwakambile wajha ali kumanjele, ‘Chokani kwanga anyimwe mwalosedwa, pitani kumoto wa muyaya waikilidwa Satana ni atumiki wake! 42Nidali ni njala anyiimwe simudanipache chakudya, nidali ni lujho anyiimwe simudanipache majhi, 43nidali mlendo anyiimwe simudanilandile, nidalibe njhalu anyiimwe simudanipache, nidali odwala ni nidali mndende anyiimwe simudajhe kuniyendela.’ 44Ndiipo naonjho siamuyanghe, ‘Ambuye, liti tidakuonani imwe muli ni njala kapina muli ni lujho kapina mwali alendo kapina mudalibe njhalu kapina muli odwala ni muli mndende sitidakutangatileni?’ 45Mfumu siwaayanghe, ‘Zene nikukambilani, ngati mudakana kwaathangatila mmojhi wa waang'ono yawa, mwanichitila ine.’ 46Anyiyawa siapelekdwe kuchilango cha muyaya, nambho anyiwajha wandhu abwino siapite ku umoyo wa muyaya.”
Currently Selected:
:
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.