YouVersion Logo
Search Icon

YESAYA 35

35
Chikondwerero cha Ziyoni m'tsogolomo
1 # Mas. 72.16 Chipululu ndi malo ouma adzakondwa; ndipo dziko loti see lidzasangalala ndi kuphuka ngati duwa. 2#Yes. 40.5; Zef. 1.7Lidzaphuka mochuluka ndi kusangalala, ngakhale kukondwa ndi kuimba; lidzapatsidwa ulemerero wa Lebanoni, ndi ukulu wa Karimele ndi Saroni; anthuwo adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wake wa Mulungu wathu.
3 # Aheb. 12.12-13 Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede. 4Nenani kwa a mitima ya chinthenthe, Limbani, musaope; taonani, Mulungu wanu adza ndi kubwezera chilango, ndi mphotho ya Mulungu; Iye adzafika ndi kukupulumutsani. 5#Mrk. 7.32-35; Yoh. 9.6-7Pamenepo maso a akhungu adzatsegudwa, ndi makutu a ogontha adzatsegulidwa. 6#Mat. 9.32-33; Yoh. 7.38-39; Mac. 3.2Pamenepo wopunduka adzatumpha ngati nswala, ndi lilime la wosalankhula lidzaimba; pakuti m'chipululu madzi adzatuluka, ndi mitsinje m'dziko loti see. 7Ndipo mchenga wong'azimira udzasanduka thamanda, ndi nthaka yopanda madzi idzasanduka zitsime zamadzi; m'malo a ankhandwe m'mene iwo anagona, mudzakhala udzu ndi mabango ndi milulu. 8#Yow. 3.17Ndipo kudzakhala khwalala kumeneko, ndi njira, ndipo idzatchedwa njira yopatulika; odetsedwa sadzapita m'menemo; koma Iye adzakhala nao oyenda m'njira, ngakhale opusa, sadzasochera m'menemo. 9#Ezk. 34.25Sikudzakhala mkango kumeneko, ngakhale chilombo cholusa sichidzapondapo, pena kupezedwa pamenepo; koma akuomboledwa adzayenda m'menemo; 10#Yes. 51.11; Chiv. 7.17; 21.4ndipo oomboledwa a Yehova adzabwera, nadzafika ku Ziyoni alikuimba; kukondwa kosatha kudzakhala pa mitu yao; iwo adzakhala ndi kusekerera ndi kukondwa, ndipo chisoni ndi kuusa moyo kudzachoka.

Currently Selected:

YESAYA 35: BLPB2014

Highlight

Share

Compare

Copy

None

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in