1
YESAYA 35:10
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
ndipo oomboledwa a Yehova adzabwera, nadzafika ku Ziyoni alikuimba; kukondwa kosatha kudzakhala pa mitu yao; iwo adzakhala ndi kusekerera ndi kukondwa, ndipo chisoni ndi kuusa moyo kudzachoka.
Compare
Explore YESAYA 35:10
2
YESAYA 35:3-4
Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede. Nenani kwa a mitima ya chinthenthe, Limbani, musaope; taonani, Mulungu wanu adza ndi kubwezera chilango, ndi mphotho ya Mulungu; Iye adzafika ndi kukupulumutsani.
Explore YESAYA 35:3-4
3
YESAYA 35:8
Ndipo kudzakhala khwalala kumeneko, ndi njira, ndipo idzatchedwa njira yopatulika; odetsedwa sadzapita m'menemo; koma Iye adzakhala nao oyenda m'njira, ngakhale opusa, sadzasochera m'menemo.
Explore YESAYA 35:8
4
YESAYA 35:5
Pamenepo maso a akhungu adzatsegudwa, ndi makutu a ogontha adzatsegulidwa.
Explore YESAYA 35:5
5
YESAYA 35:6
Pamenepo wopunduka adzatumpha ngati nswala, ndi lilime la wosalankhula lidzaimba; pakuti m'chipululu madzi adzatuluka, ndi mitsinje m'dziko loti see.
Explore YESAYA 35:6