YESAYA 12
12
Chiyamiko cha anthu a Mulungu atalangidwa
1Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mutonthoza mtima wanga. 2#Mas. 118.14Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa. 3#Yoh. 7.37-38Chifukwa chake mudzakondwera pakutunga madzi m'zitsime za chipulumutso. 4#Mas. 148.13; Yoh. 17.1, 4, 6, 26Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lake, mulalikire machitidwe ake mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lake lakwezedwa. 5#Eks. 15.1Muimbire Yehova; pakuti wachita zaulemerero; chidziwike ichi m'dziko lonse. 6Tafuula, takuwa iwe, wokhala m'Ziyoni, chifukwa Woyera wa Israele wa m'kati mwako ali wamkulu.
Currently Selected:
YESAYA 12: BLPB2014
Highlight
Share
Copy
Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi