HOSEYA 13
13
Tchimo la Israele ndi kulangidwa kwake
1 #
2Maf. 17.16, 18 Pamene Efuremu analankhula panali kunjenjemera; anadzikweza m'Israele; koma pamene anapalamula mwa Baala, anafa. 2#1Maf. 19.18; Hos. 8.4Ndipo tsopano aonjeza kuchimwa, nadzipangira mafano oyenga a siliva wao, mafano monga mwa nzeru zao, onsewo ntchito ya amisiri; anena za iwo, Anthu ophera nsembe apsompsone anaang'ombe. 3#Mas. 1.4; Hos. 6.4Chifukwa chake adzakhala ngati mtambo wa m'mawa, ndi ngati mame asansuka mamawa, ngati mungu umene mphepo iuuluza kudwale, ndi ngati utsi wotuluka kukafwambira. 4#Eks. 20.2; Yes. 43.11Koma Ine ndiye Yehova Mulungu wako chichokere m'dziko la Ejipito, ndipo suyenera kudziwa mulungu wina koma Ine; ndi popanda Ine palibe mpulumutsi. 5#Deut. 2.7Ndinakudziwa m'chipululu, m'dziko lotentha kwambiri. 6#Deut. 8.12, 14Monga mwa podyetsa pao, momwemo anakhuta; anakhuta, ndi mtima wao unakwezeka; chifukwa chake anandiiwala Ine. 7Chifukwa chake ndikhala nao ngati mkango; ngati nyalugwe ndidzalalira kunjira. 8#2Sam. 17.8Ndidzakomana nao ngati chimbalangondo chochilanda ana ake, ndi kung'amba chokuta mtima wao; ndi pomwepo ndidzawalusira ngati mkango; chilombo chidzawamwetula. 9#Deut. 33.26Israele, chikuononga ndi ichi, chakuti utsutsana ndi Ine, chithandizo chako. 10#1Sam. 8.5, 19Ili kuti mfumu yako tsopano, kuti ikupulumutse m'midzi yako yonse? Ndi oweruza ako amene unanena za iwo, Ndipatseni mfumu ndi akalonga? 11#1Sam. 8.7; 16.1Ndinakupatsa mfumu mu mkwiyo wanga; ndinamchotsanso m'ukali wanga. 12Mphulupulu ya Efuremu yamangika, tchimo lake lisungika. 13Zowawa zonga za mkazi wobala zidzamgwera, ndiye mwana wopanda nzeru; pakuti pali nyengo yakuti asachedwe mobalira ana. 14#Yes. 25.8; 1Ako. 15.54-55Ndidzawaombola kumphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako ili kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga. 15#Yer. 4.11Chinkana abala mwa abale ake, mphepo ya kum'mawa idzafika, mphepo ya Yehova yokwera kuchokera kuchipululu; ndi gwero lake lidzaphwa, ndi kasupe wake adzauma, adzafunkha chuma cha akatundu onse ofunika. 16#2Maf. 15.16; 18.11-12Samariya adzasanduka wabwinja, pakuti anapandukana ndi Mulungu wake; iwo adzagwa ndi lupanga, ana ao amakanda adzaphwanyika, ndi akazi ao okhala ndi pakati adzatumbulidwa.
Currently Selected:
HOSEYA 13: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi