1
Mk. 2:17
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Yesu atamva zimenezo adaŵayankha kuti, “Anthu amene ali bwino sasoŵa sing'anga ai, koma amene akudwala. Inetu sindidabwere kudzaitana anthu olungama, koma anthu ochimwa.”
Compare
Explore Mk. 2:17
2
Mk. 2:5
Poona chikhulupiriro chaocho, Yesu adauza munthu wa ziwalo zakufayo kuti, “Mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”
Explore Mk. 2:5
3
Mk. 2:27
Tsono Yesu popitiriza mau, adauza Afarisiwo kuti, “Mulungu adaika tsiku la Sabata kuti likhale lothandiza anthu. Sadalenge anthu kuti akhale akapolo a tsiku la Sabata ai.
Explore Mk. 2:27
4
Mk. 2:4
Koma sadathe kufika naye pafupi ndi Yesuyo chifukwa cha kuchuluka kwa anthu. Choncho adakwera pa denga, nangosasula dengalo kuyang'anana ndi pamene Yesu analiri, nkutsitsira pachiboopo machira amene adaanyamulira munthu uja.
Explore Mk. 2:4
5
Mk. 2:10-11
Koma kuti mudziŵe kuti Mwana wa Munthu ali nazo mphamvu pansi pano zokhululukira machimo, onani.” Pamenepo adauza wofa ziwalo uja kuti, “Iwe, dzuka, tenga machira ako, uzipita kumudzi.”
Explore Mk. 2:10-11
6
Mk. 2:9
Chapafupi koposa nchiti, kumuuza wa ziwalo zakufayu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Dzuka, nyamula machira ako, yamba kuyenda?’
Explore Mk. 2:9
7
Mk. 2:12
Munthu uja adadzukadi, natenga machira ake aja nkutuluka, onse aja akuwona. Anthu onse aja adazizwa kwambiri, nayamba kutamanda Mulungu nkumanena kuti, “Zoterezi ife sitinaziwone nkale lonse.”
Explore Mk. 2:12