1
Mt. 8:26
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Apo Yesu adaŵafunsa kuti, “Bwanji mukuchita mantha, inu anthu a chikhulupiriro chochepa?” Atatero adaimirira nkudzudzula mphepoyo ndi nyanjayo, kenaka padagwa bata lalikulu ndithu.
Compare
Explore Mt. 8:26
2
Mt. 8:8
Koma mkulu uja adati, “Ambuye, sindili woyenera kuti Inu nkuloŵa m'nyumba mwanga. Mungonena mau okha, ndipo wantchito wangayo achira.
Explore Mt. 8:8
3
Mt. 8:10
Yesu atamva zimenezi, adachita chidwi, ndipo adauza anthu amene ankamutsata aja kuti, “Kunena zoona, ngakhale pakati pa Aisraele sindidapeze chikhulupiriro chotere.
Explore Mt. 8:10
4
Mt. 8:13
Kenaka pouza mkulu wa asilikali uja Yesu adati, “Inu pitani bwino, zikuchitikireni monga momwe mwakhulupiriramu.” Tsono wantchito wake uja adachira nthaŵi yomweyo.
Explore Mt. 8:13
5
Mt. 8:27
Ophunzira aja adazizwa nati, “Kodi ameneyu ndi munthu wotani kuti ngakhale mphepo ndi nyanja yomwe zizimumvera?”
Explore Mt. 8:27