1
Mt. 21:22
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Ngati mukhala ndi chikhulupiriro, zonse zimene mungapemphe kwa Mulungu mudzalandira.”
Compare
Explore Mt. 21:22
2
Mt. 21:21
Yesu adati, “Ndithu ndikunenetsa kuti ngati mukhala ndi chikhulupiriro, osakayika, mudzachita zimene ndauchita mkuyuzi. Koma si pokhapo ai, ngakhale mutauza phiri ili kuti, ‘Choka apa, kadziponye m'nyanja,’ zidzachitikadi.
Explore Mt. 21:21
3
Mt. 21:9
Anthu ochuluka amene anali patsogolo, ndi amene anali m'mbuyo, adayamba kufuula kuti, “Ulemu kwa Mwana wa Davide. Ngwodala amene alikudza m'dzina la Ambuye. Ulemu kwa Mulungu kumwambamwamba.”
Explore Mt. 21:9
4
Mt. 21:13
Adaŵauza kuti, “Malembo akuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yopemphereramo.’ Koma inu mukuisandutsa phanga la achifwamba.”
Explore Mt. 21:13
5
Mt. 21:5
“Uzani mzinda wa Ziyoni kuti, ‘Ona mfumu yako ikudza kwa iwe. Ndi yodzichepetsa ndipo yakwera pa bulu. Zoonadi yakwera pa kabulu, mwana wa nyama yosenza katundu.’ ”
Explore Mt. 21:5
6
Mt. 21:42
Yesu adaŵafunsa kuti, “Kodi monga simudaŵerenge Malembo aja akuti, “ ‘Mwala umene amisiri omanga nyumba adaaukana, womwewo wasanduka mwala wapangodya, wofunika koposa. Ambuye ndiwo adachita zimenezi, ndipo nzotidabwitsa kwambiri.’
Explore Mt. 21:42
7
Mt. 21:43
“Nchifukwa chake ndikunenetsa kuti Mulungu adzakulandani Ufumu wake ndi kuupereka kwa anthu ena amene adzabala zipatso zoyenera.” [
Explore Mt. 21:43