1
Miyambo 20:22
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
Compare
Explore Miyambo 20:22
2
Miyambo 20:24
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
Explore Miyambo 20:24
3
Miyambo 20:27
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
Explore Miyambo 20:27
4
Miyambo 20:5
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
Explore Miyambo 20:5
5
Miyambo 20:19
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
Explore Miyambo 20:19
6
Miyambo 20:3
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
Explore Miyambo 20:3
7
Miyambo 20:7
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
Explore Miyambo 20:7