1
MATEYU 18:20
Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014
BLPB2014
Pakuti kumene kuli awiri kapena atatu asonkhanira m'dzina langa, ndili komweko pakati pao.
Linganisha
Chunguza MATEYU 18:20
2
MATEYU 18:19
Ndiponso ndinena kwa inu kuti ngati awiri a inu avomerezana pansi pano chinthu chilichonse akachipempha, Atate wanga wa Kumwamba adzawachitira.
Chunguza MATEYU 18:19
3
MATEYU 18:2-3
Ndipo pamene Yesu anaitana kamwana, anakaimitsa pakati pao, nati, Indetu ndinena kwa inu, Ngati simutembenuka, nimukhala monga tianato, simudzalowa konse mu Ufumu wa Kumwamba.
Chunguza MATEYU 18:2-3
4
MATEYU 18:4
Chifukwa chake yense amene adzichepetsa yekha monga kamwana aka, yemweyo ali wopambana mu Ufumu wa Kumwamba.
Chunguza MATEYU 18:4
5
MATEYU 18:5
Ndipo amene adzalandira kamwana kamodzi kotereka chifukwa cha dzina langa, alandira Ine
Chunguza MATEYU 18:5
6
MATEYU 18:18
Indetu ndinena kwa inu, Zilizonse mukazimanga pa dziko lapansi zidzakhala zomangidwa Kumwamba: ndipo zilizonse mukazimasula pa dziko lapansi, zidzakhala zomasulidwa Kumwamba.
Chunguza MATEYU 18:18
7
MATEYU 18:35
Chomwechonso Atate wanga a Kumwamba adzachitira inu, ngati inu simukhululukira yense mbale wake ndi mitima yanu.
Chunguza MATEYU 18:35
8
MATEYU 18:6
koma yense amene adzakhumudwitsa kamodzi ka tiana iti, takukhulupirira Ine, kumuyenera iye kuti mphero yaikulu ikolowekedwe m'khosi mwake, namizidwe poya pa nyanja.
Chunguza MATEYU 18:6
9
MATEYU 18:12
Nanga muyesa bwanji? Ngati munthu ali nazo nkhosa makumi khumi, ndipo ikasokera imodzi ya izo, kodi saleka zija makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi zinai, napita kumapiri, kukafuna yosokerayo?
Chunguza MATEYU 18:12
Nyumbani
Biblia
Mipango
Video