1
Mt. 27:46
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Tsono nthaŵi ili ngati 3 koloko, Yesu adafuula kwakukulu kuti, “Eli, Eli, lama sabakatani?” Ndiye kuti, “Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji?”
مقایسه
Mt. 27:46 را جستجو کنید
2
Mt. 27:51-52
Pompo chinsalu chochinga chija cha m'Nyumba ya Mulungu chidang'ambika pakatimpakati, kuyambira pamwamba mpaka pansi. Kudachita chivomezi, ndipo matanthwe adang'ambika. Manda adatsekuka ndipo anthu a Mulungu ambiri amene anali atamwalira kale, adauka kwa akufa.
Mt. 27:51-52 را جستجو کنید
3
Mt. 27:50
Koma Yesu adafuulanso kwakukulu, napereka mzimu wake.
Mt. 27:50 را جستجو کنید
4
Mt. 27:54
Mkulu wa asilikali ndiponso amene anali naye polonda Yesu, ataona chivomezi chija ndi zina zonse zimene zidaachitika, adachita mantha kwambiri nati, “Ndithudi, munthuyu adaalidi Mwana wa Mulungu.”
Mt. 27:54 را جستجو کنید
5
Mt. 27:45
Kuyambira pa 12 koloko masana mpaka pa 3 koloko, padaagwa mdima pa dziko lonse.
Mt. 27:45 را جستجو کنید
6
Mt. 27:22-23
Pilato adaŵafunsa kuti, “Nanga tsono ndichite naye chiyani Yesu, wotchedwa Khristuyu?” Anthu onse aja adati, “Apachikidwe pa mtanda!” Pilato adaŵafunsanso kuti, “Adalakwanji?” Koma anthu aja adafuula koposa kuti, “Apachikidwe pa mtanda!”
Mt. 27:22-23 را جستجو کنید