1
Mt. 10:16
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
“Mumvetse bwino! Ndikukutumani ngati nkhosa pakati pa mimbulu. Ndiye inu khalani ochenjera ngati njoka, ndi ofatsa ngati nkhunda.
مقایسه
Mt. 10:16 را جستجو کنید
2
Mt. 10:39
Munthu woyesa kusunga moyo wake, adzautaya, ndipo wotaya moyo wake chifukwa cha Ine, adzausunga.
Mt. 10:39 را جستجو کنید
3
Mt. 10:28
Musamaŵaopa amene amapha thupi, koma mzimu sangathe kuupha. Makamaka muziwopa amene angathe kuwononga thupi ndi mzimu womwe m'Gehena.
Mt. 10:28 را جستجو کنید
4
Mt. 10:38
Amene sasenza mtanda wake ndi kumanditsata, ngwosayenera kukhala wophunzira wanga.
Mt. 10:38 را جستجو کنید
5
Mt. 10:32-33
“Aliyense wondivomereza pamaso pa anthu, Inenso ndidzamuvomereza pamaso pa Atate anga amene ali Kumwamba. Koma aliyense wondikana pamaso pa anthu kuti Ine sandidziŵa, Inenso ndidzamkana pamaso pa Atate anga amene ali Kumwamba kuti sindimdziŵa.
Mt. 10:32-33 را جستجو کنید
6
Mt. 10:8
Muzikachiritsa odwala, muzikaukitsa akufa, muzikachotsa khate, muzikatulutsa mizimu yoipa. Mwalandira mwaulere, kaperekeni mwaulere.
Mt. 10:8 را جستجو کنید
7
Mt. 10:31
Choncho musati muziwopa ai. Ndinu a mtengo woposa atimba ambiri.
Mt. 10:31 را جستجو کنید
8
Mt. 10:34
“Kodi mukuyesa kuti ndidadzapereka mtendere pansi pano? Sindidadzapereke mtendere ai, koma nkhondo.
Mt. 10:34 را جستجو کنید