Alom 12
12
Ukhalo wa kumtumikila Mnungu
1Chipano, achabale wanga, pakuti Mnungu ni walisungu kupunda, nikupembhani kwa mtima wanga wonjhe, mjhichoche mwachinawene kwa Amnungu mkhale ngati njhembe yo pyeleza iyo ili yamoyo, iyo ili ya Mnungu mwene ni yomkwadilicha Mnungu. Iyi nde njila yanu ya zene yakumlambila Mnungu. 2Simudaganizila ngati wandhu ajhiko lino umo aganizila, nambho Mnungu siwakung'anamuleni maganizo yanu kwa kuganizila bwino. Pamenepo ndipo simkhoze kujhiwa icho wafuna Mnungu ni kujhiwa chindhu chili cha bwino, ilo limkwadilicha ni kuchita ngati umo ifunikila.
3Kuchokana ni ubwino uwo wanipacha Mnungu, nikukambilani anyiimwe mwaonjhe, simdajhiona kuti anyiimwe ni abwino kusiyana ni umo mmafunika kukhala. Mjhipime mwachinawene umo muli kwa chipimo cha chikhulupi icho Mnungu wamgawila kila mmojhi, 4Thupi ni limojhi ni lili ni viwalo vambili kila chiwalo chili ni jhito yake. 5Ata ngati ife ni ambili, tili thupi limojhi kwa kulunjana ni Kilisito, ni kila mmojhi ni chilunjo cha mnjake 6Chipano tili ni mbhaso zosiyana siyana kulingana ni ubwino uwo tapachidwa. Uyo wali ni mbhaso ya ulosi watumile kulingana ni chikhulupi chake. 7Uyo wali ni mbhaso ya kutumikila ni watumikile. Uyo wali ni mbhaso yoyaluza wayaluze. 8Uyo wali ni mbhaso yakwatila wina mtima wachite chimwecho. Uyo wamgawila mwina icho wali nacho wachite chimwecho kwa chikondi. Uyo waimilila waimile kwa mtima wake wonjhe, uyo wachita chindhu kwa lisungu wachite chimwecho kwa chikondi.
9Kukondana kwanu ifunika sikudakhala ni ughunghuli walionjhe. Ipilani chindhu chalichonjhe choipa, chitani vindhu vabwino. 10Kondanani anyiimwe kwa anyiimwe ni kwakonda okhulupilila achanjanu. Mumlemekeze uti kila mmojhi pakati panu. 11Msidakhala alesi kuchita jhito ya Mnungu, mchite njhito imeneyo kwa mtima onjhe ni kumtumikila Mnungu. 12Kukhulupilila kwanu kukuchiteni mkondwele ndhawi zonjhe, muembekeze mmavuto, ni kuphembela siku zonjhe. 13Mwathangatile okhulupila Mnungu achanjanu ivo savifune, alandileni alendo kwa kukondwela.
14Mwafunile ubwino yao akuchitilani voipa, mpembheni Mnungu wapache mwawi ni siwadaleswa. 15Kondwelani pamojhi ni yawo akondwela, lilani pamojhi ni yao alila. 16Mkhale kwakuvanichana bwino anyiimwe kwa anyiimwe. Simdajhidama nambho mjhichiche, mkhale ni mgwilizano apanjhi. Simdajhidama kuti muliojhiwa kupunda.
17Simdabwelezela loipa kwa loipa, chitani vindhu ivo wandhu ajhiwa kuti vabwino. 18Chitani umo ikhozekelana, mkhale kwa mtendele ni wandhu wonjhe. 19Okondedwa wanga, simdabwelezela mbwezo, nambho msiileni Mnungu chindhu chimenecho, pakuti yalembedwa mmalembo ya Mnungu, “Nghani ya kubwezela mbwezo ni njhito yanga, ine sinibwezele Ambuye akamba.” 20Yalembedwa malembo yanjake kuti, “Mdani wako wakakhala ni njala mpache chakudya, wakakhala ni lujho mpache majhi. Pakuti kwa kuchita chimwecho simwachite alenge njhoni kupunda.” 21Siudavomela kulepela ni voipa, nambho ukukhoze kuipa kwa ubwino.
Currently Selected:
Alom 12: NTNYBL2025
Highlight
Share
Copy
Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.