HOSEYA 12
12
Mlandu wa Yehova pa Israele ndi Yuda
1 #
Hos. 11.12
Efuremu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse achulukitsa mabodza ndi chipasuko, ndipo achita pangano ndi Asiriya, natenga mafuta kunka nao ku Ejipito. 2#Mik. 6.2Ndipo Yehova ali ndi mlandu ndi Yuda, nadzalanga Yakobo monga mwa njira zake, adzambwezera monga mwa machitidwe ake. 3#Gen. 25.26; 32.28M'mimba anagwira kuchitende cha mkulu wake, ndipo atakula mphamvu analimbana ndi Mulungu; 4#Gen. 28.12, 19; 32.28inde, analimbana ndi wamthenga nampambana; analira, nampembedza Iye; anampeza Iye ku Betele, ndi kumeneko Iye analankhula ndi ife; 5ndiye Yehova Mulungu wa makamu, chikumbukiro chake ndi Yehova. 6#Mik. 6.8M'mwemo utembenukire kwa Mulungu wako, sunga chifundo ndi chiweruzo, nuyembekezere Mulungu wako kosalekeza.
7 #
Miy. 11.1
Ndiye Mkanani, m'dzanja lake muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa. 8#Chiv. 3.17Ndipo Efuremu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera chuma m'ntchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala tchimo. 9Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako chichokere dziko la Ejipito, ndidzakukhalitsanso m'mahema, monga masiku a zikondwerero zoikika. 10#2Maf. 17.13Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndachulukitsa masomphenya; ndi pa dzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo. 11Kodi Giliyadi ndiye wopanda pake? Akhala achabe konse; m'Giligala aphera nsembe ya ng'ombe; inde maguwa ao a nsembe akunga miulu yamiyala m'michera ya munda. 12#Gen. 28.5; 29.20, 28Ndipo Yakobo anathawira kuthengo la Aramu, ndi Israele anagwira ntchito chifukwa cha mkazi, ndi chifukwa cha mkazi anaweta nkhosa. 13#Eks. 12.50-51Ndipo mwa mneneri Yehova anakweretsa Israele kuchokera m'Ejipito, ndi mwa mneneri anasungika. 14#2Maf. 17.11-18Efuremu wautsa mkwiyo wowawa, m'mwemo Iye adzamsiyira mwazi wake, ndi Ambuye wake adzambwezera chomtonza chake.
Currently Selected:
HOSEYA 12: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi
HOSEYA 12
12
Mlandu wa Yehova pa Israele ndi Yuda
1 #
Hos. 11.12
Efuremu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse achulukitsa mabodza ndi chipasuko, ndipo achita pangano ndi Asiriya, natenga mafuta kunka nao ku Ejipito. 2#Mik. 6.2Ndipo Yehova ali ndi mlandu ndi Yuda, nadzalanga Yakobo monga mwa njira zake, adzambwezera monga mwa machitidwe ake. 3#Gen. 25.26; 32.28M'mimba anagwira kuchitende cha mkulu wake, ndipo atakula mphamvu analimbana ndi Mulungu; 4#Gen. 28.12, 19; 32.28inde, analimbana ndi wamthenga nampambana; analira, nampembedza Iye; anampeza Iye ku Betele, ndi kumeneko Iye analankhula ndi ife; 5ndiye Yehova Mulungu wa makamu, chikumbukiro chake ndi Yehova. 6#Mik. 6.8M'mwemo utembenukire kwa Mulungu wako, sunga chifundo ndi chiweruzo, nuyembekezere Mulungu wako kosalekeza.
7 #
Miy. 11.1
Ndiye Mkanani, m'dzanja lake muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa. 8#Chiv. 3.17Ndipo Efuremu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera chuma m'ntchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala tchimo. 9Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako chichokere dziko la Ejipito, ndidzakukhalitsanso m'mahema, monga masiku a zikondwerero zoikika. 10#2Maf. 17.13Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndachulukitsa masomphenya; ndi pa dzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo. 11Kodi Giliyadi ndiye wopanda pake? Akhala achabe konse; m'Giligala aphera nsembe ya ng'ombe; inde maguwa ao a nsembe akunga miulu yamiyala m'michera ya munda. 12#Gen. 28.5; 29.20, 28Ndipo Yakobo anathawira kuthengo la Aramu, ndi Israele anagwira ntchito chifukwa cha mkazi, ndi chifukwa cha mkazi anaweta nkhosa. 13#Eks. 12.50-51Ndipo mwa mneneri Yehova anakweretsa Israele kuchokera m'Ejipito, ndi mwa mneneri anasungika. 14#2Maf. 17.11-18Efuremu wautsa mkwiyo wowawa, m'mwemo Iye adzamsiyira mwazi wake, ndi Ambuye wake adzambwezera chomtonza chake.
Currently Selected:
:
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi