YouVersion Logo
Search Icon

Hoseya 14

14
Kulapa Kubweretsa Madalitso
1Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.
Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2Bweretsani zopempha zanu
ndipo bwererani kwa Yehova.
Munene kwa Iye kuti,
“Tikhululukireni machimo athu onse
ndi kutilandira mokoma mtima,
kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3Asiriya sangatipulumutse;
ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,
sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’
kwa zimene manja athu omwe anazipanga,
pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo
ndipo ndidzawakonda mwaufulu
pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli
Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.
Adzazika mizu yake pansi
ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6mphukira zake zidzakula.
Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,
kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.
Iye adzakula bwino ngati tirigu.
Adzachita maluwa ngati mphesa
ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?
Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.
Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;
zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.
Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.
Njira za Yehova ndi zolungama;
anthu olungama amayenda mʼmenemo,
koma anthu owukira amapunthwamo.

Currently Selected:

Hoseya 14: CCL

Highlight

Share

Copy

None

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in

YouVersion uses cookies to personalize your experience. By using our website, you accept our use of cookies as described in our Privacy Policy