1
Mt. 10:16
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
“Mumvetse bwino! Ndikukutumani ngati nkhosa pakati pa mimbulu. Ndiye inu khalani ochenjera ngati njoka, ndi ofatsa ngati nkhunda.
Compare
Explore Mt. 10:16
2
Mt. 10:39
Munthu woyesa kusunga moyo wake, adzautaya, ndipo wotaya moyo wake chifukwa cha Ine, adzausunga.
Explore Mt. 10:39
3
Mt. 10:28
Musamaŵaopa amene amapha thupi, koma mzimu sangathe kuupha. Makamaka muziwopa amene angathe kuwononga thupi ndi mzimu womwe m'Gehena.
Explore Mt. 10:28
4
Mt. 10:38
Amene sasenza mtanda wake ndi kumanditsata, ngwosayenera kukhala wophunzira wanga.
Explore Mt. 10:38
5
Mt. 10:32-33
“Aliyense wondivomereza pamaso pa anthu, Inenso ndidzamuvomereza pamaso pa Atate anga amene ali Kumwamba. Koma aliyense wondikana pamaso pa anthu kuti Ine sandidziŵa, Inenso ndidzamkana pamaso pa Atate anga amene ali Kumwamba kuti sindimdziŵa.
Explore Mt. 10:32-33
6
Mt. 10:8
Muzikachiritsa odwala, muzikaukitsa akufa, muzikachotsa khate, muzikatulutsa mizimu yoipa. Mwalandira mwaulere, kaperekeni mwaulere.
Explore Mt. 10:8
7
Mt. 10:31
Choncho musati muziwopa ai. Ndinu a mtengo woposa atimba ambiri.
Explore Mt. 10:31
8
Mt. 10:34
“Kodi mukuyesa kuti ndidadzapereka mtendere pansi pano? Sindidadzapereke mtendere ai, koma nkhondo.
Explore Mt. 10:34