Yehova akuti,
“Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake,
amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize
pamene mtima wake wafulatira Yehova.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu;
iye sadzapeza zabwino.
Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi,
mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.