Sadzakutchanso “Wosiyidwa,”
ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.”
Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.”
Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.”
Chifukwa Yehova akukondwera nawe,
ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.