Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;
kupatula Ine palibenso Mulungu wina.
Ndidzakupatsa mphamvu,
ngakhale sukundidziwa Ine,
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo
anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.
Ine ndine Yehova,
ndipo palibenso wina.