1
Yesaya 14:12
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
Compare
Explore Yesaya 14:12
2
Yesaya 14:13
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
Explore Yesaya 14:13
3
Yesaya 14:14
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
Explore Yesaya 14:14
4
Yesaya 14:15
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje.
Explore Yesaya 14:15