1
Yesaya 12:2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
Compare
Explore Yesaya 12:2
2
Yesaya 12:3
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
Explore Yesaya 12:3
3
Yesaya 12:5
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Explore Yesaya 12:5
4
Yesaya 12:4
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
Explore Yesaya 12:4
5
Yesaya 12:1
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
Explore Yesaya 12:1
6
Yesaya 12:6
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Explore Yesaya 12:6