Matayo 13
13
Yaluzo la mundhu wavyala mbewu
Maluko 4:1-9; Luka 8:4-8
1Siku limwelo Yesu wadatuluka mnyumba ijha, ni kupita kukhala mbhepete mwa nyanja Galilaya, kumeneko wadakhala panjhi ni kuyaluza. 2Magulu ya wandhu yadamzungulila, ndiipo Yesu wadalamula kukwela mboti ni kukhalamo. Ndhawi imweyo wandhu wonjhe adaima mphepete mwa nyanja dala amvechele. 3Yesu wadaakambila vindhu vambili kwa chifani, niwakamba,
“Kudali ni mundhu mmojhi uyo wadapita kuvyala mbewu. 4Yapo wamamijha mbeu zina zidagwela mnjila, mbalami zidajha ni kuzidya. 5Zina zidagwela pa myala yapo palibe doti lambili. Zidamela chisanga pakuti padalibe dothi lambili. 6Jhuwa yapo lidawala, mimela idafyota ni kuuma ndande mizo yake siidapite panjhi kupunda. 7Zina zidagwela pakatikati pa minga, minga zijha zidakula ni kuzizinga ijha mimela ni kuzilepelecha kukula. 8Zina zidagwela pa dothi la chaila, zidamela, ni zidakula ni kubala, imojhi idabala njele miya, ina adabala njele sitini, ni ina adabala njele selasini.”
9Yesu wadamalizila pokamba, “Uyo wali ni makutu, yovela wavele!”
Ndande yokamba kwa vifani
Maluko 4:10-12; Luka 8:9-10
10Ndiipo oyaluzidwa wake adamchata ni adamfunjha, “Ndande yanji ukambana ni wandhu kwa vifani?”
11Yesu wadaayangha, “Anyiimwe mwachitidwa kujhiwa visisi va ufumu wa kumwamba, nambho anyiiwo sadachitidwe. 12Waliyonjhe uyo wali ni chindhu siwaongezeledwe, nambho uyo walibe kandhu, ata chaching'ono icho walinacho siwalandidwe. 13Ndendande nikamba nawo kwa chifani, pakuti apenya nambho saona, avechela nambho savela, nisaazijhiwa. 14Yakwanila kwaanyiiwo yajha wadakamba mlosi Isaya,
‘Kuvela simvele, nambho simujhiwa.
Kupenya simujhipenya, nambho simuona.
15Pakuti mitima ya wandhu yawa ni yolimba,
ayacheka makutu yawo,
athimila maso yawo.
Popande chimwecho, adakaona kwa maso yawo,
adakavela kwa makutu yawo,
adakajhiwa kwa njelu zawo,
adakanichata,
nane nidakaalamicha.’ ”
16“Nambho anyiimwe muli ni mwawi, pakuti maso yanu yapenya ni makutu yanu yavela. 17Zene nikukambilani, alosi ambili ni wandhu ambili a Mnungu adakhumbila kuyaona yajha muyaona, nambho saadayaone, ni kuyavela yajha muyavela, nambho saadayavele.”
Yesu wafotokoza mate ya chifani cha wovyala
Maluko 4:13-20; Luka 8:11-15
18“Chipano vechelani mate ya chifani cha ovyala. 19Waliyonjhe wavela mawu la Ufumu wa Mnungu ni osazindikile, wali ngati mbeu zijha zidagwa mnjila, Woipa wakujha ni kulanda chijha chavyalidwa mumtima mwake. 20Mbeu ijha idavyalidwa pa mwala ni chifani cha mundhu uyo wavela mau ni pamwepo walilandila kwa chikondwelo. 21Nambho walimbila mtima ndhawi yochepa, pakuti mau la Mnungu slidalowe kupunda mkati mwao. Mavuto kapina kusowedwa ndande ya mau yajha kukafika, wandhuwo abwelela mmbuyo nikugwa mtima. 22Mbeu ijha idavyalidwa pa minga, nde mundhu walivela mau, nambho machaucho ya jhiko ni kukhala ni khumbilo la chuma cha jhiko vilizinga mau limenelo, nisiwachita chijha Mnungu wachifuna wachichite. 23Mbeu zijha zidagwela pa ndhaka yachayila, zilingana ni mundhu uyo wavela Mawu la Mnungu, niiye wachita yayo yamkwadilicha Mnungu, ngati umo mmela umojhi uwo ubala njele miya, ni wina ubala njele sitini ni wina ubala njele selasini.”
Chifani cha matengo
24Yesu wadaakambila wandhu chifani china, “Ufumu wa kumwamba ulingana ni mundhu uyo wadavyala mbeu zabwino mmunda mwake. 25Nambho wandhu yapo adagona, mdani wake wadajha, wadavyala matengo pakati pa mapila, nikuchoka. 26Mapila yapo yadamela ni kuyamba kubala, matengo nayo yadayamba kusetela. 27Opota njhito adamchata mwene munda, adamkambila, ‘Imwe waakulu, simdavyala mbeu zabwino mmunda mwanu? Chipano matengo yachokela kuti?’ 28Iye wadayangha, ‘Mdani ndeuyo wachita chimwecho.’ Ndiipo opota njhito wake adamfunjha, ‘Bwanji, ufuna tikayazule?’ 29Iye wadaayangha, ‘Notho, msadayazula, pakuti pozula matengo, mkhoza kuzulanjho ni mapila. 30Zisiyeni zonjhe zikulile pamojhi mbaka ndhawi yokolola. Ndhawi imeneyo sinaakambile wokolola kukusa matengo akayamange machakatamachakata ni kuyabucha. Nambho mapila kololani mkaiike mnghokwe mwanga.’”
Chifani cha mbewu ya ing'ono iyo itanidwa haladali
Maluko 4:30-32; Luka 13:18-19
31Yesu wadaakambila chifani china, “Ufumu wa kumwamba ulingana ni mbeu ya ing'ono iyo itanidwa haladali iyo wadatenga mundhu mmojhi, wadaivyala mmunda mwake. 32Yene niyaying'ono kupunda kupitilila mbeu zonjhe, nambho ikaphuka ikula kupitilila mimela yonjhe. Ikula ni kukhala mtengo, ata mbalame zikujha kumanga visa mndhawi zake.”
Chifani cha amila
Luka 13:20,21
33Yesu wadaakambila chifani china, “Ufumu wa ku Mwamba uli ngati chimwechi, wamkazi mmojhi wadatenga amila, wadaisingizana ni ufa wambili wa ngano, ni wonjhe udatupa.”
Yesu wayaluza wandhu kwa vifani
Maluko 4:33-34
34Yesu wadaayaluza wandhu yaya yonjhe kwa vifani. Siwadakambenao chilichonjhe popande chifani. 35Wadachita chimwecho kuti likwanile lijha lidakambidwa ni mlosi,
“Sinikambe nao kwa chifani,
sinivumbule vindhu vobisika choka kuumbidwa kwa jhiko.”
Yesu wafotokoza mate ya chifani cha matengo
36Ndiipo Yesu wadalaila wandhu ni kulowa mnyumba. Oyaluzidwa wake adamchata, adamkambila, “Tikambile mate ya chifani cha matengo yayo yali mmunda.”
37Yesu wadaakambila, “Mundhu wadavyala mbeu zabwino mmunda, ni Mwana wa Mundhu. 38Munda ujha nde jhiko, mbeu zabwino zijha nde wandhu wajha ufumu uli wao. Nambho yajha matengo nde wana ayujha Woipa. 39Mdani uyo wadavyala matengo nde Satana. Vokolola nde kutha kwa jhiko lapanjhi, ni wokolola ni atumiki a kumwamba Amnungu. 40Ngati mujha matengo yakusidwa ni kubuchidwa moto, nde umo siyakhalilile mathelo ya jhiko. 41Mwana wa Mundhu siwaatume atumiki wake akumwamba akokole wandhu wajha waachiticha wandhu achite machimo, ni wandhu wonjhe yawo achita voipa, 42ni siwaaponye kumoto wa muyaya, uko sikukhale kulila ni kukukuta mano. 43Ndiipo wandhu abwino siawale ngati jhuwa mu Ufumu wa Atate wawo. Uyo wali ni makutu yovela wavele!”
Chifani cha chindhu cha phindhu lalikulu chabisidwa
44“Ufumu wa kumwamba ulingana ni chindhu cha phindu icho chabisidwa mmunda. Mundhu mmojhi wadachivumbula, wadachibisanjho, ni kukondwela kwa kukulu uko wadali nako, wadapita kugulicha vonjhe ivo wadalinavo, ndiipo wadabwela kugula munda ujha.”
Chifani cha mwala wa phindhu uwo utanidwa lulu
45“Ufumu wa kumwamba ulingana ni wochita malonda mmojhi uyo wamafunafuna lulu ya bwino. 46Yapo wadapeza lulu imojhi ya phindu lalikulu, wadapita kugulicha vonjhe ivo wadalinacho ni kugula lulu ijha.”
Chifani cha khokha
47“Chimchijha, ufumu wa kumwamba ulingana ni khokha ilo liponyedwa mnyanja ni kuvuwa njhomba za mitundu yosiyanasiyani. 48Khoka yapo lidajhala njhomba zambili, alovi adakokela khokha kumtunda, adakhala panjhi ni kusanghula njhomba, zabwino aziika mngwangu, nambho njhomba zoyipa adazitaya. 49Kumathelo kwa jhiko sikukhalile chimwechi, atumiki aku mwamba Amnungu siajhe nikwaapatula wandhu oyipa pakati pa wandhu abwino, 50ni wandhu oyipa saponyedwe kumoto woofya wa muyaya, uko sikukhale kulila ni kukukuta mano.”
Mayaluzo ya chipano ni ya kale
51Yesu wadafunjha, “Bwanji, mwavananavo vindhu ivi vonjhe?”
Adamuyangha, “Yetu.”
52Nayo wadaakambila, “Oyaluza walionjhe wa thauko, yapo siwang'anamuke ni kukhala oyaluzidwa wa Ufumu wa ku Mwamba, walingana ni mwene nyumba uyo wachocha chuma cha chipano ni chuma cha kale kuchokela mnghokwe yake.”
Yesu wakanidwa ku Nazaleti
Maluko 6:1-6; Luka 4:16-30
53Yesu yapo wadamaliza kukamba vifani ivi wadachoka pamalo pamenepo. 54Yapo wadafika kumujhi kwake, wadaayaluza wandhu mnyumba yokomanilana Ayahudi, niwajha adamvela adadabwa ni adajhifunjha, “Bwanji Mundhu uyu wazipata kuti njelu ni malamulo yochita vozizwicha ivi? 55Bwanji, uyu opande mwana wa osepa mitengo yokonjela vindhu? Bwanji, maye wake osati Maliya? Bwanji, abale wake osati Yakobo, Yosufu, Simoni ni Yuda? 56Bwanji, ni achabale wake, siali pamojhi ni ife pano? Bwanji wapata kuti yaya yonjhe?” 57Chimwecho adamkana.
Nambho Yesu wadaakambila, “Mlosi wapachidwa ulemu malo yonjhe, nambho siwalemekezeka kukhomo lake ni kwa wandhu a mnyumba mwake!” 58Chimwecho siwadachite vozizwicha vambili pajha ndande yosakhulupilila kwawo.
Currently Selected:
Matayo 13: NTNYBL2025
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.
Matayo 13
13
Yaluzo la mundhu wavyala mbewu
Maluko 4:1-9; Luka 8:4-8
1Siku limwelo Yesu wadatuluka mnyumba ijha, ni kupita kukhala mbhepete mwa nyanja Galilaya, kumeneko wadakhala panjhi ni kuyaluza. 2Magulu ya wandhu yadamzungulila, ndiipo Yesu wadalamula kukwela mboti ni kukhalamo. Ndhawi imweyo wandhu wonjhe adaima mphepete mwa nyanja dala amvechele. 3Yesu wadaakambila vindhu vambili kwa chifani, niwakamba,
“Kudali ni mundhu mmojhi uyo wadapita kuvyala mbewu. 4Yapo wamamijha mbeu zina zidagwela mnjila, mbalami zidajha ni kuzidya. 5Zina zidagwela pa myala yapo palibe doti lambili. Zidamela chisanga pakuti padalibe dothi lambili. 6Jhuwa yapo lidawala, mimela idafyota ni kuuma ndande mizo yake siidapite panjhi kupunda. 7Zina zidagwela pakatikati pa minga, minga zijha zidakula ni kuzizinga ijha mimela ni kuzilepelecha kukula. 8Zina zidagwela pa dothi la chaila, zidamela, ni zidakula ni kubala, imojhi idabala njele miya, ina adabala njele sitini, ni ina adabala njele selasini.”
9Yesu wadamalizila pokamba, “Uyo wali ni makutu, yovela wavele!”
Ndande yokamba kwa vifani
Maluko 4:10-12; Luka 8:9-10
10Ndiipo oyaluzidwa wake adamchata ni adamfunjha, “Ndande yanji ukambana ni wandhu kwa vifani?”
11Yesu wadaayangha, “Anyiimwe mwachitidwa kujhiwa visisi va ufumu wa kumwamba, nambho anyiiwo sadachitidwe. 12Waliyonjhe uyo wali ni chindhu siwaongezeledwe, nambho uyo walibe kandhu, ata chaching'ono icho walinacho siwalandidwe. 13Ndendande nikamba nawo kwa chifani, pakuti apenya nambho saona, avechela nambho savela, nisaazijhiwa. 14Yakwanila kwaanyiiwo yajha wadakamba mlosi Isaya,
‘Kuvela simvele, nambho simujhiwa.
Kupenya simujhipenya, nambho simuona.
15Pakuti mitima ya wandhu yawa ni yolimba,
ayacheka makutu yawo,
athimila maso yawo.
Popande chimwecho, adakaona kwa maso yawo,
adakavela kwa makutu yawo,
adakajhiwa kwa njelu zawo,
adakanichata,
nane nidakaalamicha.’ ”
16“Nambho anyiimwe muli ni mwawi, pakuti maso yanu yapenya ni makutu yanu yavela. 17Zene nikukambilani, alosi ambili ni wandhu ambili a Mnungu adakhumbila kuyaona yajha muyaona, nambho saadayaone, ni kuyavela yajha muyavela, nambho saadayavele.”
Yesu wafotokoza mate ya chifani cha wovyala
Maluko 4:13-20; Luka 8:11-15
18“Chipano vechelani mate ya chifani cha ovyala. 19Waliyonjhe wavela mawu la Ufumu wa Mnungu ni osazindikile, wali ngati mbeu zijha zidagwa mnjila, Woipa wakujha ni kulanda chijha chavyalidwa mumtima mwake. 20Mbeu ijha idavyalidwa pa mwala ni chifani cha mundhu uyo wavela mau ni pamwepo walilandila kwa chikondwelo. 21Nambho walimbila mtima ndhawi yochepa, pakuti mau la Mnungu slidalowe kupunda mkati mwao. Mavuto kapina kusowedwa ndande ya mau yajha kukafika, wandhuwo abwelela mmbuyo nikugwa mtima. 22Mbeu ijha idavyalidwa pa minga, nde mundhu walivela mau, nambho machaucho ya jhiko ni kukhala ni khumbilo la chuma cha jhiko vilizinga mau limenelo, nisiwachita chijha Mnungu wachifuna wachichite. 23Mbeu zijha zidagwela pa ndhaka yachayila, zilingana ni mundhu uyo wavela Mawu la Mnungu, niiye wachita yayo yamkwadilicha Mnungu, ngati umo mmela umojhi uwo ubala njele miya, ni wina ubala njele sitini ni wina ubala njele selasini.”
Chifani cha matengo
24Yesu wadaakambila wandhu chifani china, “Ufumu wa kumwamba ulingana ni mundhu uyo wadavyala mbeu zabwino mmunda mwake. 25Nambho wandhu yapo adagona, mdani wake wadajha, wadavyala matengo pakati pa mapila, nikuchoka. 26Mapila yapo yadamela ni kuyamba kubala, matengo nayo yadayamba kusetela. 27Opota njhito adamchata mwene munda, adamkambila, ‘Imwe waakulu, simdavyala mbeu zabwino mmunda mwanu? Chipano matengo yachokela kuti?’ 28Iye wadayangha, ‘Mdani ndeuyo wachita chimwecho.’ Ndiipo opota njhito wake adamfunjha, ‘Bwanji, ufuna tikayazule?’ 29Iye wadaayangha, ‘Notho, msadayazula, pakuti pozula matengo, mkhoza kuzulanjho ni mapila. 30Zisiyeni zonjhe zikulile pamojhi mbaka ndhawi yokolola. Ndhawi imeneyo sinaakambile wokolola kukusa matengo akayamange machakatamachakata ni kuyabucha. Nambho mapila kololani mkaiike mnghokwe mwanga.’”
Chifani cha mbewu ya ing'ono iyo itanidwa haladali
Maluko 4:30-32; Luka 13:18-19
31Yesu wadaakambila chifani china, “Ufumu wa kumwamba ulingana ni mbeu ya ing'ono iyo itanidwa haladali iyo wadatenga mundhu mmojhi, wadaivyala mmunda mwake. 32Yene niyaying'ono kupunda kupitilila mbeu zonjhe, nambho ikaphuka ikula kupitilila mimela yonjhe. Ikula ni kukhala mtengo, ata mbalame zikujha kumanga visa mndhawi zake.”
Chifani cha amila
Luka 13:20,21
33Yesu wadaakambila chifani china, “Ufumu wa ku Mwamba uli ngati chimwechi, wamkazi mmojhi wadatenga amila, wadaisingizana ni ufa wambili wa ngano, ni wonjhe udatupa.”
Yesu wayaluza wandhu kwa vifani
Maluko 4:33-34
34Yesu wadaayaluza wandhu yaya yonjhe kwa vifani. Siwadakambenao chilichonjhe popande chifani. 35Wadachita chimwecho kuti likwanile lijha lidakambidwa ni mlosi,
“Sinikambe nao kwa chifani,
sinivumbule vindhu vobisika choka kuumbidwa kwa jhiko.”
Yesu wafotokoza mate ya chifani cha matengo
36Ndiipo Yesu wadalaila wandhu ni kulowa mnyumba. Oyaluzidwa wake adamchata, adamkambila, “Tikambile mate ya chifani cha matengo yayo yali mmunda.”
37Yesu wadaakambila, “Mundhu wadavyala mbeu zabwino mmunda, ni Mwana wa Mundhu. 38Munda ujha nde jhiko, mbeu zabwino zijha nde wandhu wajha ufumu uli wao. Nambho yajha matengo nde wana ayujha Woipa. 39Mdani uyo wadavyala matengo nde Satana. Vokolola nde kutha kwa jhiko lapanjhi, ni wokolola ni atumiki a kumwamba Amnungu. 40Ngati mujha matengo yakusidwa ni kubuchidwa moto, nde umo siyakhalilile mathelo ya jhiko. 41Mwana wa Mundhu siwaatume atumiki wake akumwamba akokole wandhu wajha waachiticha wandhu achite machimo, ni wandhu wonjhe yawo achita voipa, 42ni siwaaponye kumoto wa muyaya, uko sikukhale kulila ni kukukuta mano. 43Ndiipo wandhu abwino siawale ngati jhuwa mu Ufumu wa Atate wawo. Uyo wali ni makutu yovela wavele!”
Chifani cha chindhu cha phindhu lalikulu chabisidwa
44“Ufumu wa kumwamba ulingana ni chindhu cha phindu icho chabisidwa mmunda. Mundhu mmojhi wadachivumbula, wadachibisanjho, ni kukondwela kwa kukulu uko wadali nako, wadapita kugulicha vonjhe ivo wadalinavo, ndiipo wadabwela kugula munda ujha.”
Chifani cha mwala wa phindhu uwo utanidwa lulu
45“Ufumu wa kumwamba ulingana ni wochita malonda mmojhi uyo wamafunafuna lulu ya bwino. 46Yapo wadapeza lulu imojhi ya phindu lalikulu, wadapita kugulicha vonjhe ivo wadalinacho ni kugula lulu ijha.”
Chifani cha khokha
47“Chimchijha, ufumu wa kumwamba ulingana ni khokha ilo liponyedwa mnyanja ni kuvuwa njhomba za mitundu yosiyanasiyani. 48Khoka yapo lidajhala njhomba zambili, alovi adakokela khokha kumtunda, adakhala panjhi ni kusanghula njhomba, zabwino aziika mngwangu, nambho njhomba zoyipa adazitaya. 49Kumathelo kwa jhiko sikukhalile chimwechi, atumiki aku mwamba Amnungu siajhe nikwaapatula wandhu oyipa pakati pa wandhu abwino, 50ni wandhu oyipa saponyedwe kumoto woofya wa muyaya, uko sikukhale kulila ni kukukuta mano.”
Mayaluzo ya chipano ni ya kale
51Yesu wadafunjha, “Bwanji, mwavananavo vindhu ivi vonjhe?”
Adamuyangha, “Yetu.”
52Nayo wadaakambila, “Oyaluza walionjhe wa thauko, yapo siwang'anamuke ni kukhala oyaluzidwa wa Ufumu wa ku Mwamba, walingana ni mwene nyumba uyo wachocha chuma cha chipano ni chuma cha kale kuchokela mnghokwe yake.”
Yesu wakanidwa ku Nazaleti
Maluko 6:1-6; Luka 4:16-30
53Yesu yapo wadamaliza kukamba vifani ivi wadachoka pamalo pamenepo. 54Yapo wadafika kumujhi kwake, wadaayaluza wandhu mnyumba yokomanilana Ayahudi, niwajha adamvela adadabwa ni adajhifunjha, “Bwanji Mundhu uyu wazipata kuti njelu ni malamulo yochita vozizwicha ivi? 55Bwanji, uyu opande mwana wa osepa mitengo yokonjela vindhu? Bwanji, maye wake osati Maliya? Bwanji, abale wake osati Yakobo, Yosufu, Simoni ni Yuda? 56Bwanji, ni achabale wake, siali pamojhi ni ife pano? Bwanji wapata kuti yaya yonjhe?” 57Chimwecho adamkana.
Nambho Yesu wadaakambila, “Mlosi wapachidwa ulemu malo yonjhe, nambho siwalemekezeka kukhomo lake ni kwa wandhu a mnyumba mwake!” 58Chimwecho siwadachite vozizwicha vambili pajha ndande yosakhulupilila kwawo.
Currently Selected:
:
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The New Testament in Nyanja @The Word for The World International and Nyanja Language translation, 2025. All rights reserved.