AHEBRI 13
13
1 #
Aro. 12.10
Chikondi cha pa abale chikhalebe. 2#Gen. 18.3; Mat. 25.35Musaiwale kuchereza alendo; pakuti mwa ichi ena anachereza angelo osachidziwa. 3#Mat. 25.36Kumbukirani am'nsinga, monga am'nsinga anzao; ochitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m'thupi. 4#1Ako. 6.9Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu. 5#Mat. 6.25, 34; Afi. 4.11Mtima wanu ukhale wosakonda chuma; zimene muli nazo zikukwanireni; pakuti Iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu. 6#Mas. 118.6Kotero kuti tinena molimbika mtima,
Mthandizi wanga ndiye Ambuye; sindidzaopa;
adzandichitira chiyani munthu?
7 #
Aheb. 6.12; 13.7 Kumbukirani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang'anira chitsiriziro cha mayendedwe ao mutsanze chikhulupiriro chao. 8#Yoh. 8.58; Chiv. 1.4Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse. 9#Aef. 4.14; Aro. 14.17Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo. 10#1Ako. 9.13Tili nalo guwa la nsembe, limene iwo akutumikira chihema alibe ulamuliro wa kudyako.
11 #
Eks. 29.14
Pakuti matupi a nyama zija, mwazi wa izo umatengedwa, ndi mkulu wa ansembe kulowa m'malo opatulidwa, chifukwa cha zoipa, amatenthedwa kunja kwa tsasa. 12#Yoh. 19.17-18Mwa ichi Yesunso, kuti akayeretse anthuwo mwa mwazi wa Iye yekha, adamva chowawa kunja kwa chipata. 13#1Pet. 4.14Chifukwa chake titulukire kwa Iye kunja kwa tsasa osenza tonzo lake. 14#Aheb. 11.10Pakuti pano tilibe mudzi wokhalitsa, komatu tifunafuna ulinkudzawo. 15#Mas. 50.14Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake. 16#Aro. 12.13Koma musaiwale kuchitira chokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulungu akondwera nazo. 17#1Ate. 5.12; Mac. 20.26, 28Mverani atsogoleri anu, nimuwagonjere; pakuti alindirira moyo wanu, monga akuwerengera; kuti akachite ndi chimwemwe, osati mwachisoni: pakuti ichi sichikupindulitsani inu.
18 #
Akol. 4.3; 2Ako. 1.12 Mutipempherere ife; pakuti takopeka mtima kuti tili nacho chikumbu mtima chokoma m'zonse, pofuna kukhala nao makhalidwe abwino. 19Ndipo ndikudandaulirani koposa kuchita ichi, kuti kubwera kwanga kwa inu kufulumidwe.
20 #
Aro. 12.10; Ezk. 37.24; Yoh. 10.11, 14; Aheb. 10.29 Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye wotuluka mwa akufa Mbusa wamkulu wa nkhosa ndi mwazi wa chipangano chosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu, 21#Afi. 2.13akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.
22Koma ndidandaulira inu, abale, lolani mau a chidandauliro; pakutinso ndalembera inu mwachidule. 23#1Ate. 3.2Zindikirani kuti mbale wathu Timoteo wamasulidwa; pamodzi ndi iye, ngati akudza msanga, ndidzakuonani inu.
24 #
Aheb. 7.17
Perekani moni kwa atsogoleri anu onse, ndi oyera mtima onse. Akupatsani moni iwo a ku Italiya.
25Chisomo chikhale ndi inu nonse, Amen.
Currently Selected:
AHEBRI 13: BLPB2014
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi
AHEBRI 13
13
1 #
Aro. 12.10
Chikondi cha pa abale chikhalebe. 2#Gen. 18.3; Mat. 25.35Musaiwale kuchereza alendo; pakuti mwa ichi ena anachereza angelo osachidziwa. 3#Mat. 25.36Kumbukirani am'nsinga, monga am'nsinga anzao; ochitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m'thupi. 4#1Ako. 6.9Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu. 5#Mat. 6.25, 34; Afi. 4.11Mtima wanu ukhale wosakonda chuma; zimene muli nazo zikukwanireni; pakuti Iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu. 6#Mas. 118.6Kotero kuti tinena molimbika mtima,
Mthandizi wanga ndiye Ambuye; sindidzaopa;
adzandichitira chiyani munthu?
7 #
Aheb. 6.12; 13.7 Kumbukirani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang'anira chitsiriziro cha mayendedwe ao mutsanze chikhulupiriro chao. 8#Yoh. 8.58; Chiv. 1.4Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse. 9#Aef. 4.14; Aro. 14.17Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo. 10#1Ako. 9.13Tili nalo guwa la nsembe, limene iwo akutumikira chihema alibe ulamuliro wa kudyako.
11 #
Eks. 29.14
Pakuti matupi a nyama zija, mwazi wa izo umatengedwa, ndi mkulu wa ansembe kulowa m'malo opatulidwa, chifukwa cha zoipa, amatenthedwa kunja kwa tsasa. 12#Yoh. 19.17-18Mwa ichi Yesunso, kuti akayeretse anthuwo mwa mwazi wa Iye yekha, adamva chowawa kunja kwa chipata. 13#1Pet. 4.14Chifukwa chake titulukire kwa Iye kunja kwa tsasa osenza tonzo lake. 14#Aheb. 11.10Pakuti pano tilibe mudzi wokhalitsa, komatu tifunafuna ulinkudzawo. 15#Mas. 50.14Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake. 16#Aro. 12.13Koma musaiwale kuchitira chokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulungu akondwera nazo. 17#1Ate. 5.12; Mac. 20.26, 28Mverani atsogoleri anu, nimuwagonjere; pakuti alindirira moyo wanu, monga akuwerengera; kuti akachite ndi chimwemwe, osati mwachisoni: pakuti ichi sichikupindulitsani inu.
18 #
Akol. 4.3; 2Ako. 1.12 Mutipempherere ife; pakuti takopeka mtima kuti tili nacho chikumbu mtima chokoma m'zonse, pofuna kukhala nao makhalidwe abwino. 19Ndipo ndikudandaulirani koposa kuchita ichi, kuti kubwera kwanga kwa inu kufulumidwe.
20 #
Aro. 12.10; Ezk. 37.24; Yoh. 10.11, 14; Aheb. 10.29 Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye wotuluka mwa akufa Mbusa wamkulu wa nkhosa ndi mwazi wa chipangano chosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu, 21#Afi. 2.13akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.
22Koma ndidandaulira inu, abale, lolani mau a chidandauliro; pakutinso ndalembera inu mwachidule. 23#1Ate. 3.2Zindikirani kuti mbale wathu Timoteo wamasulidwa; pamodzi ndi iye, ngati akudza msanga, ndidzakuonani inu.
24 #
Aheb. 7.17
Perekani moni kwa atsogoleri anu onse, ndi oyera mtima onse. Akupatsani moni iwo a ku Italiya.
25Chisomo chikhale ndi inu nonse, Amen.
Currently Selected:
:
Highlight
Share
Copy

Want to have your highlights saved across all your devices? Sign up or sign in
The Bible in Chichewa Published as Buku Lopatulika
Bible Society of Malawi