1
Mk. 11:24
Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa
BLY-DC
Nchifukwa chake ndikukuuzani kuti, m'mapemphero mwanu mukapempha Mulungu chinthu chilichonse, muzikhulupirira kuti mwalandira, ndipo mudzachilandiradi.
Compare
Explore Mk. 11:24
2
Mk. 11:23
Ndithu ndikunenetsa kuti aliyense wolamula phiri ili kuti, ‘Choka apa, kadziponye m'nyanja,’ atanena ndi mtima wosakayika, nakhulupirira ndithu kuti zimene akunenazo zichitikadi, ndithu zidzachitikadi monga momwe waneneramo.
Explore Mk. 11:23
3
Mk. 11:25
Ndipo pamene mukuti mupemphere, muziyamba mwakhululukira mnzanu ngati muli naye nkanthu. Mukatero, Atate anunso amene ali Kumwamba adzakukhululukirani machimo anu.” [
Explore Mk. 11:25
4
Mk. 11:22
Yesu adaŵayankha kuti, “Muzikhala ndi chikhulupiriro mwa Mulungu.
Explore Mk. 11:22
5
Mk. 11:17
Pambuyo pake adayamba kuŵaphunzitsa naŵauza kuti, “Paja Malembo akuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba yopemphereramo anthu a mitundu yonse.’ Koma inu mwaisandutsa phanga la achifwamba.”
Explore Mk. 11:17
6
Mk. 11:9
Anthu amene adaali patsogolo, ndi amene adaali m'mbuyo, adayamba kufuula kuti, “Ulemu kwa Mulungu. Ngwodala amene alikudza m'dzina la Ambuye.
Explore Mk. 11:9
7
Mk. 11:10
Udalitsidwe Ufumu wa atate athu Davide umene ulikudza tsopano. Ulemu kwa Mulungu kumwambamwamba.”
Explore Mk. 11:10