1
Marko 14:36
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Iye anati, “Abba, Atate, zinthu zonse ndi zotheka ndi Inu. Chotsereni chikhochi. Komabe chitani zimene Inu mukufuna, osati zimene Ine ndikufuna.”
Compare
Explore Marko 14:36
2
Marko 14:38
Khalani tcheru ndi kupemphera kuti musalowe mʼmayesero. Mzimu ukufuna, koma thupi ndi lofowoka.”
Explore Marko 14:38
3
Marko 14:9
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse, zimene wachitazi zidzanenedwa pomukumbukira iye.”
Explore Marko 14:9
4
Marko 14:34
Iye anawawuza kuti, “Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo musagone.”
Explore Marko 14:34
5
Marko 14:22
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, ili ndi thupi langa.”
Explore Marko 14:22
6
Marko 14:23-24
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo. Iye anawawuza kuti, “Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri.
Explore Marko 14:23-24
7
Marko 14:27
Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “ ‘Kantha Mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
Explore Marko 14:27
8
Marko 14:42
Nyamukani! Tiyeni tizipita! Uyu wondipereka Ine wafika!”
Explore Marko 14:42
9
Marko 14:30
Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”
Explore Marko 14:30