1
Mateyu 26:41
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
Compare
Explore Mateyu 26:41
2
Mateyu 26:38
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
Explore Mateyu 26:38
3
Mateyu 26:39
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
Explore Mateyu 26:39
4
Mateyu 26:28
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
Explore Mateyu 26:28
5
Mateyu 26:26
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
Explore Mateyu 26:26
6
Mateyu 26:27
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
Explore Mateyu 26:27
7
Mateyu 26:40
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
Explore Mateyu 26:40
8
Mateyu 26:29
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
Explore Mateyu 26:29
9
Mateyu 26:75
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.
Explore Mateyu 26:75
10
Mateyu 26:46
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
Explore Mateyu 26:46
11
Mateyu 26:52
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
Explore Mateyu 26:52