“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli,
bwererani kwa Ine,”
akutero Yehova.
“Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga
ndipo musasocherenso.
Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo
kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’
Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse
ndipo adzanditamanda.”