“Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri
zingachititse iwe kukhala mfumu?
Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa.
Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera,
ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa,
ndipo zonse zinkamuyendera bwino.
Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?”
akutero Yehova.