Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,
motero kuti amamutumikira Iye,
amakonda dzina la Yehova,
amamugwirira ntchito,
komanso kusunga Sabata osaliyipitsa
ndi kusunga bwino pangano langa,
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,
ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.
Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo
ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.
Paja nyumba yanga idzatchedwa
nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”