Angathe kuti ndi amene amachita zolungama
ndi kuyankhula zoona,
amene amakana phindu lolipeza monyenga
ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu,
amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo
ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,
kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri.
Azidzalandira chakudya chake
ndipo madzi sadzamusowa.