1
Yesaya 26:3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
CCL
Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
Compare
Explore Yesaya 26:3
2
Yesaya 26:4
Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Explore Yesaya 26:4
3
Yesaya 26:9
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
Explore Yesaya 26:9
4
Yesaya 26:12
Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
Explore Yesaya 26:12
5
Yesaya 26:8
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
Explore Yesaya 26:8
6
Yesaya 26:7
Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
Explore Yesaya 26:7
7
Yesaya 26:5
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
Explore Yesaya 26:5
8
Yesaya 26:2
Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
Explore Yesaya 26:2