Tsono Yehova anandiyankha, nati:
“Lemba masomphenyawa
ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale
kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake;
masomphenyawa akunena zamʼtsogolo
ndipo sizidzalephera kuchitika.
Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere;
zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.